< Rute 3 >

1 Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino?
And Naomi her mother-in-law said to her, My daughter, shall I not seek rest for thee, that it may be well with thee?
2 Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira.
And now is not Boaz our kinsman, with whose maidens thou were? Behold, he winnows barley tonight in the threshing-floor.
3 Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa.
Wash thyself therefore, and anoint thee, and put thy raiment upon thee, and get thee down to the threshing-floor. But do not make thyself known to the man until he shall have done eating and drinking.
4 Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”
And it shall be, when he lies down, that thou shall notice the place where he shall lie. And thou shall go in, and uncover his feet, and lie thee down. And he will tell thee what thou shall do.
5 Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”
And she said to her, All that thou say I will do.
6 Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.
And she went down to the threshing-floor, and did according to all that her mother-in-law bade her.
7 Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.
And when Boaz had eaten and drunk, and his heart was merry, he went to lie down at the end of the heap of grain. And she came softly, and uncovered his feet, and laid down.
8 Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.
And it came to pass at midnight, that the man was startled, and turned himself, and, behold, a woman lay at his feet.
9 Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”
And he said, Who are thou? And she answered, I am Ruth thy handmaid. Spread therefore thy skirt over thy handmaid, for thou are a near kinsman.
10 Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka.
And he said, Blessed be thou of Jehovah, my daughter. Thou have shown more kindness in the latter end than at the beginning, inasmuch as thou did not follow young men, whether poor or rich.
11 Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino.
And now, my daughter, fear not. I will do to thee all that thou say, for all the city of my people know that thou are a worthy woman.
12 Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine.
And now it is true that I am a near kinsman. However there is a kinsman nearer than I.
13 Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”
Remain this night, and it shall be in the morning that if he will perform to thee the part of a kinsman, well; let him do the kinsman's part. But if he will not do the part of a kinsman to thee, then I will do the part of a kinsman to thee, as Jehovah lives. Lie down until the morning.
14 Choncho Rute anagona ku mapazi ake mpaka mmawa, koma anadzuka mmamawa kusanayere chifukwa Bowazi anati, “Aliyense asadziwe kuti kopondera barele kunabwera mkazi.”
And she lay at his feet until the morning. And she rose up before one could discern another. For he said, Let it not be known that the woman came to the threshing-floor.
15 Bowazi anati kwa Rute, “Bwera nacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.
And he said, Bring the mantle that is upon thee, and hold it. And she held it, and he measured six measures of barley, and laid it on her, and he went into the city.
16 Rute atafika kwa apongozi ake anamufunsa kuti, “Zinayenda bwanji mwana wanga?” Kenaka iye anafotokoza zonse zimene Bowazi anamuchitira.
And when she came to her mother-in-law, she said, Who are thou, my daughter? And she told her all that the man had done to her.
17 Ndipo anati, “Munthuyo anandipatsa makilogalamu makumi awiri awa a barele, nandiwuza kuti usapite kwa apongozi ako wopanda kanthu.”
And she said, He gave me these six measures of barley, for he said, Go not empty to thy mother-in-law.
18 Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”
Then she said, Sit still, my daughter, until thou know how the matter will fall, for the man will not rest until he has finished the thing this day.

< Rute 3 >