< Aroma 2 >

1 Choncho, iwe amene umaweruza munthu wina, ulibe pokanira pakuti nthawi iliyonse pamene uweruza wina ukudzitsutsa wekha chifukwa iwe amene umaweruzawe umachitanso zinthu zomwezo.
C'est pourquoi tu es sans excuse, ô homme, quel que soit celui qui juge. Car dans ce que tu juges un autre, tu te condamnes toi-même. Car toi qui juges, tu pratiques les mêmes choses.
2 Tsopano ife tikudziwa kuti chiweruzo cha Mulungu, chotsutsa amene amachita zinthu zotere, nʼchokhazikika pa choonadi.
Nous savons que le jugement de Dieu est conforme à la vérité contre ceux qui pratiquent de telles choses.
3 Kodi ukuganiza kuti udzathawa chiweruzo cha Mulungu iwe munthu wamba, pamene uweruza ena, iwe ndi kumachitanso zomwezo?
Penses-tu, ô homme qui juge ceux qui pratiquent de telles choses, et qui fais de même, que tu échapperas au jugement de Dieu?
4 Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa Mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirira kwake? Kodi sukuzindikira kuti kukoma mtima kwakeko, nʼkofuna kuti iweyo ulape machimo ako?
Ou bien méprises-tu les richesses de sa bonté, de sa longanimité et de sa patience, ne sachant pas que la bonté de Dieu vous conduit à la repentance?
5 Koma pakuti ndiwe wosamvera ndi wa mtima wosafuna kulapa, ukudzisungira chilango pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu, pamene chiweruzo cholungama cha Mulungu chidzaonetsedwa.
Mais selon votre dureté et votre impénitence, vous vous réservez la colère au jour de la fureur, de la révélation et du juste jugement de Dieu,
6 Mulungu adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake.
qui « rendra à chacun selon ses œuvres ».
7 Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. (aiōnios g166)
à ceux qui, par la persévérance dans la bonne action, recherchent la gloire, l'honneur et l'incorruptibilité, la vie éternelle; (aiōnios g166)
8 Koma Mulungu adzakhuthulira mkwiyo ndi ukali wake pa amene amachita zofuna zawo ndi kukana choonadi nʼkumatsatira zoyipa.
mais à ceux qui se complaisent dans l'égoïsme et n'obéissent pas à la vérité, mais obéissent à l'injustice, il y aura de la colère, de l'indignation,
9 Masautso ndi zowawa zidzagwera munthu aliyense amene amachita zonyansa, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
de l'oppression et de l'angoisse sur toute âme d'homme qui fait le mal, au Juif d'abord, et aussi au Grec.
10 Koma ulemerero, ulemu ndi mtendere zidzakhala kwa aliyense amene amachita zabwino, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
Mais la gloire, l'honneur et la paix vont à tout homme qui fait le bien, au Juif d'abord, et aussi au Grec.
11 Pajatu Mulungu alibe tsankho.
Car il n'y a pas de partialité chez Dieu.
12 Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo.
En effet, tous ceux qui ont péché sans la loi périront aussi sans la loi. Tous ceux qui ont péché sous la loi seront jugés par la loi.
13 Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama.
Car ce ne sont pas ceux qui écoutent la loi qui sont justes devant Dieu, mais ceux qui la mettent en pratique qui seront justifiés
14 Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo.
(car lorsque les païens qui n'ont pas la loi font par nature les choses de la loi, ceux-là, n'ayant pas la loi, sont une loi pour eux-mêmes,
15 Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza.
en ce qu'ils montrent l'œuvre de la loi écrite dans leur cœur, leur conscience en rendant témoignage avec eux, et leurs pensées entre eux les accusant ou bien les excusant)
16 Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.
au jour où Dieu jugera les secrets des hommes, selon ma Bonne Nouvelle, par Jésus-Christ.
17 Koma iweyo, amene umadzitcha kuti ndiwe Myuda, umadalira Malamulo, ndipo umanyadira ubale wako ndi Mulungu,
En effet, tu portes le nom de Juif, tu te reposes sur la loi, tu te glorifies en Dieu,
18 ngati umadziwa chifuniro chake, ndi kudziwa zoyenera kuchita chifukwa unaphunzitsidwa ndi Malamulo;
tu connais sa volonté, et tu approuves les choses excellentes, étant instruit par la loi,
19 ngati umadziwadi kuti ndiwe mtsogoleri wa osaona, nyale yowunikira amene ali mu mdima,
et tu as l'assurance d'être toi-même un guide des aveugles, une lumière pour ceux qui sont dans les ténèbres,
20 mlangizi wa anthu opusa, mphunzitsi wa makanda, chifukwa umadziwa kuti mʼMalamulo uli nayo nzeru yonse ndi choonadi,
un correcteur des insensés, un éducateur de bébés, ayant dans la loi la forme de la connaissance et de la vérité.
21 tsono, iwe amene umaphunzitsa ena, sudziphunzitsa wekha kodi? Kodi iwe amene umalalikira kuti anthu asabe, umabanso?
Toi donc qui enseignes un autre, n'enseignes-tu pas toi-même? Toi qui prêches que l'homme ne doit pas voler, voles-tu?
22 Kodi iwe amene umanena kuti anthu asachite chigololo, umachitanso chigololo? Kodi iwe amene umanyasidwa ndi mafano, umalandanso za mʼnyumba zopembedzera mafanowo?
Vous qui dites que l'homme ne doit pas commettre d'adultère, commettez-vous l'adultère? Vous qui avez en horreur les idoles, pillez-vous les temples?
23 Kodi iwe amene umadzitama ndi Malamulo, umamuchititsa manyazi Mulungu posamvera Malamulowo?
Vous qui vous glorifiez de la loi, déshonorez-vous Dieu en désobéissant à la loi?
24 Monga kwalembedwa, “Dzina la Mulungu likuchitidwa chipongwe pakati pa a mitundu ina chifukwa cha inu.”
Car « le nom de Dieu est blasphémé parmi les païens à cause de vous », comme il est écrit.
25 Mdulidwe umakhala ndi phindu ngati usunga Malamulo, koma ngati sumvera Malamulo, iweyo umakhala ngati kuti sunachite mdulidwe.
En effet, la circoncision est utile, si tu mets la loi en pratique; mais si tu transgresses la loi, ta circoncision est devenue incirconcision.
26 Ngati amene sanachite mdulidwe achita zomwe zili mʼMalamulo, kodi sadzatengedwa ngati ochita mdulidwe?
Si donc l'incirconcis observe les ordonnances de la loi, son incirconcision ne sera-t-elle pas considérée comme une circoncision?
27 Munthu amene sanachite mdulidwe mʼthupi koma amamvera Malamulo adzakutsutsa iwe wosamvera Malamulowe, ngakhale kuti uli nawo Malamulo olembedwawo.
Ceux qui sont physiquement incirconcis, mais qui accomplissent la loi, ne te jugeront-ils pas, toi qui, avec la lettre et la circoncision, es un transgresseur de la loi?
28 Myuda weniweni si amene angooneka ngati Myuda pamaso pa anthu, ndipo mdulidwe weniweni si umene umangochitika mʼthupi pamaso pa anthu.
Car n'est pas Juif celui qui l'est extérieurement, ni la circoncision extérieure dans la chair;
29 Ayi, Myuda weniweni ndi amene ali Myuda mu mtima mwake, ndipo mdulidwe weniweni ndi wa mtima, wochitika ndi Mzimu, osati ndi malamulo olembedwa. Woyamikira munthu wotere ndi Mulungu, osati anthu ayi.
mais est Juif celui qui l'est intérieurement, et la circoncision est celle du cœur, de l'esprit, non de la lettre, dont la louange ne vient pas des hommes, mais de Dieu.

< Aroma 2 >