< Aroma 2 >

1 Choncho, iwe amene umaweruza munthu wina, ulibe pokanira pakuti nthawi iliyonse pamene uweruza wina ukudzitsutsa wekha chifukwa iwe amene umaweruzawe umachitanso zinthu zomwezo.
Therefore thou art inexcusable, O man, whoever thou art, that judgest: for wherein thou judgest another, thou condemnest thyself; for thou that judgest dost the same things.
2 Tsopano ife tikudziwa kuti chiweruzo cha Mulungu, chotsutsa amene amachita zinthu zotere, nʼchokhazikika pa choonadi.
But we know that the judgement of God is according to truth against those that do such things.
3 Kodi ukuganiza kuti udzathawa chiweruzo cha Mulungu iwe munthu wamba, pamene uweruza ena, iwe ndi kumachitanso zomwezo?
And thinkest thou, O man, who judgest those that do such things, and dost the same, that thou shalt escape the judgement of God?
4 Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa Mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirira kwake? Kodi sukuzindikira kuti kukoma mtima kwakeko, nʼkofuna kuti iweyo ulape machimo ako?
Or despisest thou the riches of his goodness, and forbearance, and long-suffering, not knowing that the goodness of God leadeth thee to repentance?
5 Koma pakuti ndiwe wosamvera ndi wa mtima wosafuna kulapa, ukudzisungira chilango pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu, pamene chiweruzo cholungama cha Mulungu chidzaonetsedwa.
But by thy hardness and impenitence of heart thou art treasuring up to thyself wrath against the day of wrath and revelation of the just judgement of God,
6 Mulungu adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake.
who will render to every one according to his works:
7 Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. (aiōnios g166)
to them, who by perseverance in well-doing seek for glory, and honor, and immortality, eternal life: (aiōnios g166)
8 Koma Mulungu adzakhuthulira mkwiyo ndi ukali wake pa amene amachita zofuna zawo ndi kukana choonadi nʼkumatsatira zoyipa.
but to those who are contentious, and obey not the truth, but obey unrighteousness, indignation and wrath.
9 Masautso ndi zowawa zidzagwera munthu aliyense amene amachita zonyansa, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
Tribulation and anguish shall be upon every soul of man that worketh evil, both of the Jew, and of the Gentile:
10 Koma ulemerero, ulemu ndi mtendere zidzakhala kwa aliyense amene amachita zabwino, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
but glory, and honor, and peace to every one that worketh good, both to the Jew, and to the Greek:
11 Pajatu Mulungu alibe tsankho.
for there is no respect of persons with God.
12 Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo.
For as many as have sinned without the law shall also perish without the law; and as many as have sinned under the law shall be judged by the law;
13 Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama.
(for not the hearers of the law are just before God, but the doers of the law shall be justified:
14 Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo.
for when the Gentiles, who have not the law, do by nature the duties of the law, these though they have not the law, are a law to themselves,
15 Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza.
and shew the work of the law written on their hearts, their conscience witnessing together with it, and their own thoughts either accusing, or excusing them, )
16 Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.
in the day when God will judge the secrets of men by Jesus Christ, according to my gospel.
17 Koma iweyo, amene umadzitcha kuti ndiwe Myuda, umadalira Malamulo, ndipo umanyadira ubale wako ndi Mulungu,
Behold thou art called a Jew, and restest on the law, and boastest in God,
18 ngati umadziwa chifuniro chake, ndi kudziwa zoyenera kuchita chifukwa unaphunzitsidwa ndi Malamulo;
and knowest his will, and approvest things that are excellent, being instructed out of the law,
19 ngati umadziwadi kuti ndiwe mtsogoleri wa osaona, nyale yowunikira amene ali mu mdima,
and art persuaded that thou art a guide of the blind,
20 mlangizi wa anthu opusa, mphunzitsi wa makanda, chifukwa umadziwa kuti mʼMalamulo uli nayo nzeru yonse ndi choonadi,
a light to them that are in the darkness, an instructor of the simple, a teacher of babes, having the form of the knowledge and of the truth which is in the law.
21 tsono, iwe amene umaphunzitsa ena, sudziphunzitsa wekha kodi? Kodi iwe amene umalalikira kuti anthu asabe, umabanso?
Thou then, who teachest another, teachest thou not thyself? Thou, that preachest a man should not steal, dost thou steal?
22 Kodi iwe amene umanena kuti anthu asachite chigololo, umachitanso chigololo? Kodi iwe amene umanyasidwa ndi mafano, umalandanso za mʼnyumba zopembedzera mafanowo?
Thou, that sayest a man should not commit adultery, dost thou commit adultery? Thou, that abhorrest idols, dost thou commit sacrilege?
23 Kodi iwe amene umadzitama ndi Malamulo, umamuchititsa manyazi Mulungu posamvera Malamulowo?
Thou, that boastest in the law, dost thou by transgression of the law dishonour God?
24 Monga kwalembedwa, “Dzina la Mulungu likuchitidwa chipongwe pakati pa a mitundu ina chifukwa cha inu.”
for through you the name of God is blasphemed among the Gentiles, as it is written.
25 Mdulidwe umakhala ndi phindu ngati usunga Malamulo, koma ngati sumvera Malamulo, iweyo umakhala ngati kuti sunachite mdulidwe.
For circumcision indeed is profitable, if thou keep the law: but if thou be a transgressor of the law, thy circumcision is become uncircumcision.
26 Ngati amene sanachite mdulidwe achita zomwe zili mʼMalamulo, kodi sadzatengedwa ngati ochita mdulidwe?
Therefore if the uncircumcised keep the righteous precepts of the law, shall not his uncircumcision be accounted to him for circumcision?
27 Munthu amene sanachite mdulidwe mʼthupi koma amamvera Malamulo adzakutsutsa iwe wosamvera Malamulowe, ngakhale kuti uli nawo Malamulo olembedwawo.
and shall not the uncircumcision that is by nature, if it fulfil the law, judge thee, who by the letter and circumcision art a transgressor of the law? for he is not a Jew, who is only so in appearance;
28 Myuda weniweni si amene angooneka ngati Myuda pamaso pa anthu, ndipo mdulidwe weniweni si umene umangochitika mʼthupi pamaso pa anthu.
nor is that circumcision, which is only in appearance, in the flesh;
29 Ayi, Myuda weniweni ndi amene ali Myuda mu mtima mwake, ndipo mdulidwe weniweni ndi wa mtima, wochitika ndi Mzimu, osati ndi malamulo olembedwa. Woyamikira munthu wotere ndi Mulungu, osati anthu ayi.
but he is a Jew who is one inwardly, and circumcision is that of the heart in the spirit, not in the letter: whose praise is not from men, but from God.

< Aroma 2 >