< Masalimo 99 >

1 Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
L’Éternel règne: que les peuples tremblent! Il est assis entre les chérubins: que la terre s’émeuve!
2 Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
L’Éternel est grand en Sion, et il est haut élevé par-dessus tous les peuples.
3 Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
Ils célébreront ton nom grand et terrible: – il est saint! –
4 Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
Et la force du roi qui aime la justice. Toi, tu établis la droiture, tu exerces le jugement et la justice en Jacob.
5 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
Exaltez l’Éternel, notre Dieu, et prosternez-vous devant le marchepied de ses pieds: – il est saint!
6 Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
Moïse et Aaron, parmi ses sacrificateurs, et Samuel, parmi ceux qui invoquent son nom, crièrent à l’Éternel, et il leur a répondu.
7 Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
Il leur parla dans la colonne de nuée: ils ont gardé ses témoignages, et le statut qu’il leur avait donné.
8 Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
Éternel, notre Dieu! tu leur as répondu, tu as été pour eux un Dieu qui pardonnait, et prenait vengeance de leurs actes.
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
Exaltez l’Éternel, notre Dieu, et prosternez-vous en la montagne de sa sainteté; car l’Éternel, notre Dieu, est saint!

< Masalimo 99 >