< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
Yahweh, God who avenges, God who avenges, shine over us.
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Rise up, judge of the earth, give to the proud what they deserve.
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
How long will the wicked, Yahweh, how long will the wicked rejoice?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
They pour out their arrogant words; all those who do evil boast.
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
They crush your people, Yahweh; they afflict the nation that belongs to you.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
They kill the widow and foreigner who lives in their country, and they murder the fatherless.
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
They say, “Yahweh will not see, the God of Jacob does not take notice of it.”
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Understand, you stupid people! You fools, when will you ever learn?
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
He who made the ear, does he not hear? He who formed the eye, does he not see?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
He who disciplines the nations, does he not correct? He is the one who gives knowledge to man.
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
Yahweh knows the thoughts of men, that they are vapor.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Blessed is the one whom you instruct, Yahweh, the one whom you teach from your law.
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
You give him rest in times of trouble until a pit is dug for the wicked.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
For Yahweh will not forsake his people or abandon his inheritance.
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
For judgment will again be righteous; and all the upright in heart will follow it.
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Who will rise up to defend me against the evildoers? Who will stand up for me against the wicked?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
Unless Yahweh had been my help, I would soon be lying down in the place of silence.
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
When I said, “My foot is slipping,” Your covenant faithfulness, Yahweh, held me up.
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
When cares within me are many, your consolations make me happy.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Can a throne of destruction be allied with you, one who creates injustice by statute?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
They conspire together to take the life of the righteous and they condemn the innocent to death.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
But Yahweh has been my high tower, and my God has been the rock of my refuge.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
He will bring on them their own iniquity and will cut them off in their own wickedness. Yahweh our God will cut them off.

< Masalimo 94 >