< Masalimo 94 >

1 Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
A Psalm of David for the fourth [day] of the week. The Lord is a God of vengeance; the God of vengeance has declared himself.
2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
Be thou exalted, thou that judgest the earth: render a reward to the proud.
3 Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
How long shall sinners, O Lord, how long shall sinners boast?
4 Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
They will utter and speak unrighteousness; all the workers of iniquity will speak [so].
5 Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
They have afflicted thy people, O Lord, and hurt thine heritage.
6 Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
They have slain the widow and fatherless, and murdered the stranger.
7 Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
And they said, The Lord shall not see, neither shall the God of Jacob understand.
8 Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
Understand now, ye simple among the people; and ye fools, at length be wise.
9 Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
He that planted the ear, does he not hear? or he that formed the eye, does not he perceive?
10 Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
He that chastises the heathen, shall not he punish, [even] he that teaches man knowledge?
11 Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
The Lord knows the thoughts of men, that they are vain.
12 Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
Blessed is the man whomsoever thou shalt chasten, O Lord, and shalt teach him out of thy law;
13 mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
to give him rest from evil days, until a pit be digged for the sinful one.
14 Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
For the Lord will not cast off his people, neither will he forsake his inheritance;
15 Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
until righteousness return to judgment, and all the upright in heart shall follow it. (Pause)
16 Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
Who will rise up for me against the transgressors? or who will stand up with me against the workers of iniquity?
17 Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
If the Lord had not helped me, my soul had almost sojourned in Hades.
18 Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
If I said, My foot has been moved;
19 Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
thy mercy, O Lord, helped me. O Lord, according to the multitude of my griefs within my heart, thy consolation have soothed my soul.
20 Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
Shall the throne of iniquity have fellowship with thee, which frames mischief by an ordinance?
21 Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
They will hunt for the soul of the righteous, and condemn innocent blood.
22 Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
But the Lord was my refuge; and my God the helper of my hope.
23 Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.
And he will recompense to them their iniquity and their wickedness: the Lord our God shall utterly destroy them.

< Masalimo 94 >