< Masalimo 92 >

1 Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
A psalm. A song; for the sabbath day. It is good to give thanks to the Lord, to sing praise to your name, O Most High,
2 Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
to declare your love in the morning, and your faithfulness in the night,
3 kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
with voice and a ten-stringed harp, with music that throbs on the lyre.
4 Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
For you make me glad by your deeds, Lord, at the work of your hands I will ring out my joy.
5 Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
How great are your works, O Lord; how deep are your thoughts!
6 Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
The insensitive cannot know, nor can a fool understand,
7 kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
that, though the wicked flourish like grass, and evildoers all blossom, they will perish forever.
8 Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
But you are exalted forever.
9 Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
For see! Your enemies, Lord For see! Your enemies perish, all evildoers are scattered.
10 Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
But you lift me to honour, and anoint me afresh with oil.
11 Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
My eyes will feast on my foes, and my ears will hear of the doom of the wicked.
12 Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
The righteous will sprout like the palm, will grow like a cedar of Lebanon.
13 odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
In the house of the Lord are they planted, in the courts of our God they will sprout.
14 Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
They will still bear fruit in old age, all sappy and fresh will they be
15 kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”
So they proclaim the Lord to be just, my rock, in whom is no wrong.

< Masalimo 92 >