< Masalimo 91 >

1 Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
He that dwellith in the help of the hiyeste God; schal dwelle in the proteccioun of God of heuene.
2 Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.”
He schal seie to the Lord, Thou art myn vptaker, and my refuit; my God, Y schal hope in him.
3 Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa;
For he delyuered me fro the snare of hunteris; and fro a scharp word.
4 Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
With hise schuldris he schal make schadowe to thee; and thou schalt haue hope vnder hise fetheris.
5 Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,
His treuthe schal cumpasse thee with a scheld; thou schalt not drede of nyytis drede.
6 kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
Of an arowe fliynge in the dai, of a gobelyn goynge in derknessis; of asailing, and a myddai feend.
7 Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
A thousynde schulen falle doun fro thi side, and ten thousynde fro thi riytside; forsothe it schal not neiye to thee.
8 Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
Netheles thou schalt biholde with thin iyen; and thou schalt se the yelding of synneris.
9 Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
For thou, Lord, art myn hope; thou hast set thin help altherhiyeste.
10 Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
Yuel schal not come to thee; and a scourge schal not neiye to thi tabernacle.
11 Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
For God hath comaundid to hise aungels of thee; that thei kepe thee in alle thi weies.
12 ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
Thei schulen beere thee in the hondis; leste perauenture thou hirte thi foot at a stoon.
13 Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
Thou schalt go on a snake, and a cocatrice; and thou schalt defoule a lioun and a dragoun.
14 “Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
For he hopide in me, Y schal delyuere hym; Y schal defende him, for he knew my name.
15 Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
He criede to me, and Y schal here him, Y am with him in tribulacioun; Y schal delyuere him, and Y schal glorifie hym.
16 Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”
I schal fille hym with the lengthe of daies; and Y schal schewe myn helthe to him.

< Masalimo 91 >