< Masalimo 9 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
Przewodnikowi chóru, na Halmutlabben. Pieśń Dawida. Będę [cię] wysławiał, PANIE, całym mym sercem; będę opowiadał o wszystkich twoich cudach.
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
Będę się cieszył i radował tobą, będę śpiewał twemu imieniu, o Najwyższy!
3 Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
Gdy cofną się moi nieprzyjaciele, upadną i znikną sprzed twego oblicza.
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
Ty bowiem przeprowadziłeś mój sąd i moją sprawę, zasiadłeś na tronie jako sędzia sprawiedliwy.
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
Skarciłeś pogan, wytraciłeś niegodziwych, wymazałeś ich imię na wieki wieków.
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
O nieprzyjacielu, twoje spustoszenia skończyły się na zawsze, zburzyłeś miasta, ich pamięć przepadła razem z nimi.
7 Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
Ale PAN trwa na wieki, ustawił swój tron, by sądzić.
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
On będzie sądził świat sprawiedliwie, osądzi narody według słuszności.
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
I będzie PAN ucieczką dla uciśnionego, schronieniem w czasie niedoli.
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
I będą ufać tobie ci, którzy znają twoje imię, bo nie opuszczasz, PANIE, tych, którzy cię szukają.
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
Śpiewajcie PANU, który mieszka na Syjonie, opowiadajcie wśród narodów o jego dziełach.
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
Bo on dopomina się krwi i pamięta o nich, a nie zapomina wołania strapionych.
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
Zmiłuj się nade mną, PANIE, spójrz, jak mnie uciskają ci, którzy mnie nienawidzą, ty, który podnosisz mnie z bram śmierci;
14 kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
Abym głosił wszelką twą chwałę w bramach córki Syjonu; będę się radował twoim zbawieniem.
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
Poganie wpadli w dół, [który] wykopali; w sidłach, które zastawili, uwięzła ich noga.
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
PAN dał się poznać, gdy odbył sąd, w dzieła swoich rąk uwikłał się niegodziwy. (Higgajon, Sela)
17 Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
Niegodziwi zstąpią do piekła, wszystkie narody, które zapominają Boga. (Sheol h7585)
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
Bo biedak nie będzie zapomniany na zawsze, nadzieja ubogich nie zginie na wieki.
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
Powstań, PANIE, niech nie triumfuje człowiek, niech narody zostaną osądzone przed twoim obliczem.
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)
PANIE, ześlij na nie strach, aby narody poznały, że są tylko ludźmi. (Sela)

< Masalimo 9 >