< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
Pieśń wyuczająca podana Asafowi. Słuchaj, ludu mój! zakonu mego; nakłońcież uszów swych do słów ust moich.
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
Otworzę w podobieństwie usta moje, a będę opowiadał przypowiastki starodawne.
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
Cośmy słyszeli, i poznali, i co nam ojcowie nasi opowiadali.
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
Nie zataimy tego przed synami ich, którzy przyszłym potomkom swoim opowiadać będą chwały Pańskie, i moc jego, i cuda jego, które uczynił.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
Bo wzbudził świadectwo w Jakóbie, a zakon wydał w Izraelu; przykazał ojcom naszym, aby to do wiadomości podawali synom swoim,
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
Aby poznał wiek potomny, synowie, którzy się narodzić mieli, a oni zaś powstawszy, aby to opowiadali synom swoim;
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
Aby pokładali w Bogu nadzieję swoję, a nie zapominali na sprawy Boże, ale strzegli przykazań jego;
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
Aby się nie stali jako ojcowie ich narodem odpornym i nieposłusznym, narodem, który nie wygotował serca swego, aby był wierny Bogu duch jego.
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
Albo jako synowie Efraimowi zbrojni, którzy, choć umieli z łuku strzelać, wszakże w dzień wojny tył podali.
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
Bo nie przestrzegali przymierza Bożego, a według zakonu jego zbraniali się chodzić.
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
Zapomnieli na sprawy jego, i na dziwne dzieła jego, które im pokazywał.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
Przed ojcami ich czynił cuda w ziemi Egipskiej, na polu Soan.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
Rozdzielił morze, i przeprowadził ich, i sprawił, że stanęły wody jako kupa.
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
Prowadził ich w obłoku we dnie, a każdej nocy w jasnym ogniu.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
Rozszczepił skały na puszczy, a napoił ich, jako z przepaści wielkich.
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
Wywiódł strumienie ze skały, a uczynił, że wody ciekły jako rzeki.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
A wszakże oni przyczynili grzechów przeciwko niemu, a wzruszyli Najwyższego na puszczy do gniewu;
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
I kusili Boga w sercu swem, żądając pokarmu według lubości swojej.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
A mówili przeciwko Bogu temi słowy: Izali może Bóg zgotować stół na tej puszczy?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
Oto uderzył w skałę, a wypłynęły wody, i rzeki wezbrały; izali też będzie mógł dać chleb? Izali nagotuje mięsa ludowi swemu?
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
Przetoż usłyszawszy to Pan, rozgniewał się, a ogień się zapalił przeciw Jakóbowi, także i popędliwość powstała przeciw Izraelowi;
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
Przeto, iż nie wierzyli Bogu, a nie mieli nadziei w zbawieniu jego.
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
Choć był rozkazał obłokom z góry, i forty niebieskie otworzył.
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
I spuścił im jako deszcz mannę ku pokarmowi, a pszenicę niebieską dał im.
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Chleb mocarzów jadł człowiek, a zesłał im pokarmów do sytości.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
Obrócił wiatr ze wschodu na powietrzu, a przywiódł mocą swą wiatr z południa;
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
I spuścił na nich mięso jako proch, i ptastwo skrzydlate jako piasek morski;
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
Spuścił je w pośród obozu ich, wszędy około namiotów ich.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
I jedli, a nasyceni byli hojnie, i dał im, czego żądali.
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
A gdy jeszcze nie wypełnili żądości swej, gdy jeszcze pokarm był w ustach ich:
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
Tedy zapalczywość Boża przypadła na nich, i pobił tłustych ich, a przedniejszych z Izraela poraził.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
Ale w tem wszystkiem jeszcze grzeszyli, i nie wierzyli cudom jego;
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
Przetoż sprawił, że marnie dokonali dni swoich, i lat swoich w strachu.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
Gdy ich tracił, jeźliże go szukali, i nawracali się, a szukali z rana Boga,
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
Przypominając sobie, iż Bóg był skałą ich, a Bóg najwyższy odkupicielem ich:
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
(Aczkolwiek pochlebiali mu usty swemi, i językiem swoim kłamali mu;
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
A serce ich nie było szczere przed nim, ani wiernymi byli w przymierzu jego.)
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
On jednak będąc miłosierny odpuszczał nieprawości ich, a nie zatracał ich, ale częstokroć odwracał gniew swój, a nie pobudzał wszystkiego gniewu swego;
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
Bo pamiętał, że są ciałem, wiatrem, który odchodzi, a nie wraca się zaś.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
Jako go często draźnili na puszczy, i do boleści przywodzili na pustyniach?
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
Bo coraz kusili Boga, a Świętemu Izraelskiemu granice zamierzali.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
Nie pamiętali na rękę jego, i na on dzień, w który ich wybawił z utrapienia;
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
Gdy czynił w Egipcie znaki swoje, a cuda swe na polu Soan;
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
Gdy obrócił w krew rzeki ich, i strumienie ich, tak, że z nich pić nie mogli.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
Przepuścił na nich rozmaite muchy, aby ich kąsały, i żaby, aby ich gubiły:
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
I dał chrząszczom urodzaje ich, a prace ich szarańczy.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
Potłukł gradem szczepy ich, a drzewa leśnych fig ich gradem lodowym.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
I podał gradowi bydło ich, a majętność ich węglu ognistemu.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
Posłał na nich gniew zapalczywości swojej, popędliwość, i rozgniewanie, i uciśnienie, przypuściwszy na nich aniołów złych.
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
Wyprostował ścieżkę gniewowi swemu, nie zachował od śmierci duszy ich, i na bydło ich powietrze dopuścił;
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
I pobił wszystko pierworodztwo w Egipcie, pierwiastki mocy ich w przybytkach Chamowych;
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
Ale jako owce wyprowadził lud swój, a wodził ich jako stada po puszczy.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
Wodził ich w bezpieczeństwie, tak, że się nie lękali, (a nieprzyjaciół ich okryło morze, )
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
Aż ich przywiódł do świętej granicy swojej, na onę górę, której nabyła prawica jego.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
I wyrzucił przed twarzą ich narody, i sprawił, że im przyszły na sznur dziedzictwa ich, ażeby mieszkały w przybytkach ich pokolenia Izraelskie.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
A wszakże przecież kusili i draźnili Boga najwyższego, a świadectwa jego nie strzegli.
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
Ale się odwrócili, i przewrotnie się obchodzili, jako i ojcowie ich; wywrócili się jako łuk omylny.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
Bo go wzruszyli do gniewu wyżynami swemi, a rytemi bałwanami swemi pobudzili go do zapalczywości.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
Co słysząc Bóg rozgniewał się, i zbrzydził sobie bardzo Izraela,
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
Tak, że opuściwszy przybytek w Sylo, namiot, który postawił między ludźmi,
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
Podał w niewolę moc swoję, i sławę swoję w ręce nieprzyjacielskie.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
Dał pod miecz lud swój, a na dziedzictwo swoje rozgniewał się.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
Młodzieńców jego ogień pożarł, a panienki jego nie były uczczone.
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
Kapłani jego od miecza polegli, a wdowy jego nie płakały.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
Lecz potem ocucił się Pan jako ze snu, jako mocarz wykrzykający od wina.
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
I zaraził nieprzyjaciół swoich na pośladkach, a na wieczną hańbę podał ich.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
Ale choć wzgardził namiotem Józefowym, a pokolenia Efraimowego nie obrał,
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
Wszakże obrał pokolenie Judowe, i górę Syon, którą umiłował.
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
I wystawił sobie jako pałac wysoki świątnicę swoję, jako ziemię, którą ugruntował na wieki.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
I obrał Dawida sługę swego, wziąwszy go z obór owczych;
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
Gdy chodził za owcami kotnemi, przyprowadził go, aby pasł Jakóba, lud jego, i Izraela, dziedzictwo jego;
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
Który ich pasł w szczerości serca swego, a w roztropności rąk swoich prowadził ich.

< Masalimo 78 >