< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
A maskil of Asaph. My people, attend to my teaching: bend your ears to the words of my mouth,
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
as I open my mouth in a poem on the riddling story of the past.
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
What we have heard and known, and what our ancestors have told us,
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
we will not hide from their children. We will tell to the next generation the praises and might of the Lord, and the wonders that he has done.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
He set up a testimony in Jacob, a law he appointed in Israel, which he commanded our ancestors to make known to their children,
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
that the next generation should know it, that the children yet to be born should arise and tell their children;
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
that in God they might put their confidence, and not forget God’s works; but that they might keep his commandments,
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
and not be like their ancestors, a generation defiant and stubborn, a generation with heart unsteady, and spirit unfaithful towards God.
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
Ephraimites, armed bowmen, turned back in the day of battle.
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
They did not keep God’s covenant, they refused to walk in his law.
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
They forgot what he had done, and the wonders he had shown them.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
He did wonders before their ancestors in the country of Zoan in Egypt.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
Through the sea which he split he brought them, making waters stand up like a heap;
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
he led them by day with a cloud, all the night with a light of fire.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
From the rocks which he split in the wilderness, he gave them to drink as of ocean’s abundance.
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
He brought streams out of the rock, and made water run down like rivers.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
Yet they still went on sinning against him, they defied the Most High in the desert.
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
They wilfully challenged God, demanding the food that they longed for.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
‘Is God able,’ such was their challenge, ‘to spread in the desert a table?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
From the rock that he struck there gushed water, and torrents that overflowed; but can he also give bread, or provide his people with meat?’
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
When the Lord heard this, he was furious, and fire was kindled on Jacob, anger flared up against Israel.
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
For they put no trust in God, no confidence in his help.
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
So he summoned the clouds above; and, opening the doors of heaven,
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
he rained manna upon them for food, and grain of heaven he gave them.
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Everyone ate the bread of angels; he sent them food to the full.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
He launched the east wind in the heavens, and guided the south by his power.
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
He rained meat upon them like dust, winged bird like the sand of the sea.
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
In the midst of their camp he dropped it, all around their tents.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
They ate and were more than filled; he had brought them the thing they desired.
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
But the thing they desired became loathsome: while their food was still in their mouths,
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
the wrath of God rose against them. He slew the stoutest among them, and laid low the young men of Israel.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
Yet for all this they sinned yet more, and refused to believe in his wonders.
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
So he ended their days in a breath, and their years in sudden dismay.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
When he slew them, then they sought after him, they turned and sought God with diligence.
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
They remembered that God was their rock, and the Most High God their redeemer.
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
But they flattered him with their mouth, and lied to him with their tongue.
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
Their heart was not steady with him, they were faithless to his covenant.
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
But he is full of pity: he pardons sin and destroys not. Often he turns his anger away, without stirring his wrath at all.
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
So he remembered that they were but flesh, breath that passes and does not return.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
But how often they rebelled in the desert, and caused him grief in the wilderness,
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
tempting God again and again, provoking the Holy One of Israel.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
They did not remember his strength, nor the day he redeemed from the foe,
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
how he set his signs in Egypt, in the country of Zoan his wonders.
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
He turned their canals into blood, their streams undrinkable.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
He sent forth flies, which devoured them; frogs, too, which destroyed them.
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
Their crops he gave to the caterpillar, and the fruits of their toil to the locust.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
He slew their vines with hail, and their sycamore trees with frost.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
He delivered their cattle to the hail, and their flocks to bolts of fire.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
He let loose his hot anger among them, fury and wrath and distress, a band of destroying angels.
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
He cleared a path for his anger, did not spare them from death, but gave them over to pestilence.
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
He struck down all the firstborn in Egypt, the first fruits of their strength in the tents of Ham.
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
He led forth his people like sheep, he was guide to his flock in the desert.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
Securely he led them, and free from fear, while their foes were drowned in the sea.
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
To his holy realm he brought them, to the mountain his right hand had purchased.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
He drove out the nations before them, and allotted their land for possession, and their tents for Israel to live in.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
Yet they tempted and angered the Most High God, they did not observe his decrees.
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
They drew back, false like their ancestors; they failed like a treacherous bow.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
Their shrines stirred him to anger, their idols moved him to jealousy.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
When God heard of this, he was furious, and he spurned Israel utterly.
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
He abandoned his home in Shiloh, the tent he had pitched among people.
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
He gave his strength up to captivity, his glory to the hands of the foe.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
He gave his people to the sword, he was furious with his own.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
Fire devoured their young men, and their maidens had no marriage-song.
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
Their priests fell by the sword, and their widows could not weep.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
Then the Lord awoke as from sleep, like a warrior flushed with wine;
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
and he beat back his foes, putting them to perpetual scorn.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
He disowned the tent of Joseph, he rejected the tribe of Ephraim;
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
but he chose the tribe of Judah, Mount Zion, which he loves.
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
And he built like the heights his sanctuary, like the earth which he founded forever.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
And he chose David his servant, taking him from the sheepfolds.
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
From the mother-ewes he brought him, to be shepherd to Jacob his people, and to Israel his inheritance.
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
With upright heart did he shepherd them, and with skilful hands did he guide them.

< Masalimo 78 >