< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
[A contemplation by Asaph.] Hear my teaching, my people. Turn your ears to the words of my mouth.
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
I will open my mouth in a parable. I will utter dark sayings since the beginning of the world,
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
which we have heard and known, and our fathers have told us.
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
We will not hide them from their descendants, telling to the generation to come the praises of the LORD, his strength, and his wondrous works that he has done.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
For he established a testimony in Jacob, and appointed a teaching in Israel, which he commanded our fathers, that they should make them known to their children;
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
that the generation to come might know it, the children yet unborn, and arise and tell their children,
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
that they might set their hope in God, and not forget the works of God, but keep his commandments,
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
and might not be as their fathers, a stubborn and rebellious generation, a generation that did not make their hearts loyal, whose spirit was not steadfast with God.
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
The people of Ephraim, being armed and carrying bows, turned back in the day of battle.
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
They did not keep God's covenant, and refused to walk by his Law.
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
They forgot his doings, his wondrous works that he had shown them.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
He did marvelous things in the sight of their fathers, in the land of Egypt, in the field of Zoan.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
He split the sea, and caused them to pass through. He made the waters stand as a heap.
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
In the daytime he also led them with a cloud, and all night with a light of fire.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
He split rocks in the wilderness, and gave them drink abundantly as out of the depths.
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
He brought streams also out of the rock, and caused waters to run down like rivers.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
Yet they still went on to sin against him, to rebel against the Most High in the desert.
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
They tempted God in their heart by asking food according to their desire.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
Yes, they spoke against God. They said, "Can God prepare a table in the wilderness?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
Look, he struck the rock, so that waters gushed out, and streams overflowed. Can he give bread also? Will he provide flesh for his people?"
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
Therefore the LORD heard, and was angry. A fire was kindled against Jacob, anger also went up against Israel,
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
because they did not believe in God, and did not trust in his salvation.
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
Yet he commanded the clouds above, and opened the doors of heaven.
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
He rained down manna on them to eat, and gave them bread from heaven.
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Man ate the bread of the mighty ones. He sent them food to the full.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
He caused the east wind to blow in the sky. By his power he guided the south wind.
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
He rained also flesh on them as the dust; winged birds as the sand of the seas.
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
He let it fall in the midst of his camp, all around his tent.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
So they ate, and were well filled. He gave them their own desire.
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
They did not turn from their cravings. Their food was yet in their mouths,
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
when the anger of God went up against them, killed some of the fattest of them, and struck down the young men of Israel.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
For all this they still sinned, and did not believe in his wondrous works.
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
Therefore he consumed their days in vanity, and their years in terror.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
When he killed them, then they inquired after him. They returned and sought God earnestly.
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
They remembered that God was their rock, the Most High God, their redeemer.
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
But they flattered him with their mouth, and lied to him with their tongue.
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
For their heart was not right with him, neither were they faithful in his covenant.
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
But he, being merciful, forgave iniquity, and did not destroy them. Yes, many times he turned his anger away, and did not stir up all his wrath.
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
He remembered that they were but flesh, a wind that passes away, and doesn't come again.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
How often they rebelled against him in the wilderness, and grieved him in the desert.
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
They turned again and tempted God, and gave pain to the Holy One of Israel.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
They did not remember his hand, nor the day when he redeemed them from the adversary;
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
how he set his signs in Egypt, his wonders in the field of Zoan,
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
he turned their rivers into blood, and their streams, so that they could not drink.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
He sent among them swarms of flies, which devoured them; and frogs, which destroyed them.
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
He gave also their increase to the caterpillar, and their labor to the locust.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
He destroyed their vines with hail, their sycamore fig trees with frost.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
He gave over their livestock also to the hail, and their flocks to hot thunderbolts.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
He threw on them the fierceness of his anger, wrath, indignation, and trouble, and a band of destroying angels.
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
He made a path for his anger. He did not spare their soul from death, but gave their life over to the pestilence,
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
and struck all the firstborn in Egypt, the chief of their strength in the tents of Ham.
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
But he led forth his own people like sheep, and guided them in the wilderness like a flock.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
He led them safely, so that they weren't afraid, but the sea overwhelmed their enemies.
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
He brought them to the border of his sanctuary, to this mountain, which his right hand had taken.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
He also drove out the nations before them, allotted them for an inheritance by line, and made the tribes of Israel to dwell in their tents.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
Yet they tempted and rebelled against the Most High God, and did not keep his testimonies;
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
but turned back, and dealt treacherously like their fathers. They were turned aside like a deceitful bow.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
For they provoked him to anger with their high places, and moved him to jealousy with their engraved images.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
When God heard this, he was angry, and greatly abhorred Israel;
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
So that he forsook the tabernacle at Shiloh, the tent where he dwelt among men;
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
and delivered his strength into captivity, his glory into the adversary's hand.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
He also gave his people over to the sword, and was angry with his inheritance.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
Fire devoured their young men. Their virgins had no wedding song.
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
Their priests fell by the sword, and their widows couldn't weep.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
Then the Lord awakened as one out of sleep, like a mighty man who shouts by reason of wine.
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
He struck his adversaries backward. He made them a permanent shame.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
Moreover he rejected the tent of Joseph, and did not choose the tribe of Ephraim,
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
But chose the tribe of Judah, Mount Zion which he loved.
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
He built his sanctuary like the heights, like the earth which he has established forever.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
He also chose David his servant, and took him from the sheepfolds;
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
from following the ewes that have their young, he brought him to be the shepherd of Jacob his servant, and Israel his inheritance.
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
So he was their shepherd according to the integrity of his heart, and guided them by the skillfulness of his hands.

< Masalimo 78 >