< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
亚萨的训诲诗。 我的民哪,你们要留心听我的训诲, 侧耳听我口中的话。
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
我要开口说比喻; 我要说出古时的谜语,
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
是我们所听见、所知道的, 也是我们的祖宗告诉我们的。
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
我们不将这些事向他们的子孙隐瞒, 要将耶和华的美德和他的能力, 并他奇妙的作为,述说给后代听。
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
因为,他在雅各中立法度, 在以色列中设律法; 是他吩咐我们祖宗要传给子孙的,
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
使将要生的后代子孙可以晓得; 他们也要起来告诉他们的子孙,
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
好叫他们仰望 神, 不忘记 神的作为, 惟要守他的命令。
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
不要像他们的祖宗, 是顽梗悖逆、居心不正之辈, 向着 神,心不诚实。
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
以法莲的子孙带着兵器,拿着弓, 临阵之日转身退后。
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
他们不遵守 神的约, 不肯照他的律法行;
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
又忘记他所行的 和他显给他们奇妙的作为。
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
他在埃及地,在琐安田, 在他们祖宗的眼前施行奇事。
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
他将海分裂,使他们过去, 又叫水立起如垒。
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
他白日用云彩, 终夜用火光引导他们。
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
他在旷野分裂磐石, 多多地给他们水喝,如从深渊而出。
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
他使水从磐石涌出, 叫水如江河下流。
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
他们却仍旧得罪他, 在干燥之地悖逆至高者。
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
他们心中试探 神, 随自己所欲的求食物,
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
并且妄论 神说: 神在旷野岂能摆设筵席吗?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
他曾击打磐石,使水涌出,成了江河; 他还能赐粮食吗? 还能为他的百姓预备肉吗?
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
所以,耶和华听见就发怒; 有烈火向雅各烧起; 有怒气向以色列上腾;
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
因为他们不信服 神, 不倚赖他的救恩。
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
他却吩咐天空, 又敞开天上的门,
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
降吗哪,像雨给他们吃, 将天上的粮食赐给他们。
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
各人吃大能者的食物; 他赐下粮食,使他们饱足。
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
他领东风起在天空, 又用能力引了南风来。
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
他降肉,像雨在他们当中,多如尘土, 又降飞鸟,多如海沙,
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
落在他们的营中, 在他们住处的四面。
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
他们吃了,而且饱足; 这样就随了他们所欲的。
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
他们贪而无厌, 食物还在他们口中的时候,
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
神的怒气就向他们上腾, 杀了他们内中的肥壮人, 打倒以色列的少年人。
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
虽是这样,他们仍旧犯罪, 不信他奇妙的作为。
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
因此,他叫他们的日子全归虚空, 叫他们的年岁尽属惊恐。
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
他杀他们的时候,他们才求问他, 回心转意,切切地寻求 神。
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
他们也追念 神是他们的磐石, 至高的 神是他们的救赎主。
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
他们却用口谄媚他, 用舌向他说谎。
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
因他们的心向他不正, 在他的约上也不忠心。
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
但他有怜悯, 赦免他们的罪孽, 不灭绝他们, 而且屡次消他的怒气, 不发尽他的忿怒。
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
他想到他们不过是血气, 是一阵去而不返的风。
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
他们在旷野悖逆他, 在荒地叫他担忧,何其多呢!
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
他们再三试探 神, 惹动以色列的圣者。
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
他们不追念他的能力 和赎他们脱离敌人的日子;
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
他怎样在埃及地显神迹, 在琐安田显奇事,
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
把他们的江河并河汊的水都变为血, 使他们不能喝。
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
他叫苍蝇成群落在他们当中,嘬尽他们, 又叫青蛙灭了他们,
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
把他们的土产交给蚂蚱, 把他们辛苦得来的交给蝗虫。
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
他降冰雹打坏他们的葡萄树, 下严霜打坏他们的桑树,
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
又把他们的牲畜交给冰雹, 把他们的群畜交给闪电。
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
他使猛烈的怒气和忿怒、恼恨、苦难 成了一群降灾的使者,临到他们。
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
他为自己的怒气修平了路, 将他们交给瘟疫, 使他们死亡,
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
在埃及击杀一切长子, 在含的帐棚中击杀他们强壮时头生的。
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
他却领出自己的民如羊, 在旷野引他们如羊群。
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
他领他们稳稳妥妥地,使他们不致害怕; 海却淹没他们的仇敌。
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
他带他们到自己圣地的边界, 到他右手所得的这山地。
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
他在他们面前赶出外邦人, 用绳子将外邦的地量给他们为业, 叫以色列支派的人住在他们的帐棚里。
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
他们仍旧试探、悖逆至高的 神, 不守他的法度,
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
反倒退后,行诡诈,像他们的祖宗一样; 他们改变,如同翻背的弓。
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
因他们的邱坛惹了他的怒气; 因他们雕刻的偶像触动他的愤恨。
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
神听见就发怒, 极其憎恶以色列人。
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
甚至他离弃示罗的帐幕, 就是他在人间所搭的帐棚;
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
又将他的约柜交与人掳去, 将他的荣耀交在敌人手中;
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
并将他的百姓交与刀剑, 向他的产业发怒。
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
少年人被火烧灭; 处女也无喜歌。
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
祭司倒在刀下, 寡妇却不哀哭。
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
那时,主像世人睡醒, 像勇士饮酒呼喊。
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
他就打退了他的敌人, 叫他们永蒙羞辱;
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
并且他弃掉约瑟的帐棚, 不拣选以法莲支派,
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
却拣选犹大支派—他所喜爱的锡安山;
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
盖造他的圣所,好像高峰, 又像他建立永存之地;
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
又拣选他的仆人大卫, 从羊圈中将他召来,
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
叫他不再跟从那些带奶的母羊, 为要牧养自己的百姓雅各 和自己的产业以色列。
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
于是,他按心中的纯正牧养他们, 用手中的巧妙引导他们。

< Masalimo 78 >