< Masalimo 77 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
Przewodnikowi chóru dla Jedutuna. Psalm Asafa. [Wzniosłem] swój głos do Boga i zawołałem; [wzniosłem] swój głos do Boga i mnie wysłuchał.
2 Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
W dniu mego utrapienia szukałem Pana, moje ręce wyciągałem w nocy nieustannie, moja dusza nie dała się pocieszyć.
3 Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
Gdy wspominałem Boga, byłem strwożony; rozmyślałem, a mój duch był ogarnięty utrapieniem. (Sela)
4 Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
Ty zatrzymujesz otwarte powieki mych oczu, jestem [tak] zaniepokojony, że nie potrafię mówić.
5 Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
Rozpamiętuję dni przeszłe [i] dawne lata.
6 Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
Przypominam sobie mój śpiew; nocą rozmyślam w sercu i mój duch docieka:
7 “Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
Czy Pan odrzuci na wieki i już więcej nie okaże łaski?
8 Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
Czy jego miłosierdzie ustało na zawsze i jego obietnica nigdy się nie spełni?
9 Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
Czy Bóg zapomniał o litości? Czy w gniewie stłumił swoją łaskawość? (Sela)
10 Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
I powiedziałem: To jest moja niemoc; [jednak będę wspominał] lata prawicy Najwyższego.
11 Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
Będę wspominał dzieła PANA, będę wspominał twoje dawne cuda.
12 Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
Będę rozmyślał o wszystkich twoich dziełach i o twoich czynach będę mówił.
13 Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
Boże, święta jest twoja droga; który bóg jest tak wielki, jak [nasz] Bóg?
14 Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
Ty [jesteś] Bogiem, który czyni cuda; dałeś poznać narodom swoją moc.
15 Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
Odkupiłeś [swoim] ramieniem twój lud, synów Jakuba i Józefa. (Sela)
16 Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
Widziały cię wody, o Boże, widziały cię wody [i] ulękły się, poruszyły się głębiny.
17 Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
Chmury spłynęły wodą, niebiosa wydały gromy i poleciały twoje strzały.
18 Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
Huk twego grzmotu wśród obłoków, błyskawice oświetliły świat, ziemia poruszyła się i zatrzęsła.
19 Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
Twoja droga [wiodła] przez morze, twoje ścieżki przez wielkie wody i nie było znać twoich śladów.
20 Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.
Prowadziłeś swój lud jak stado owiec ręką Mojżesza i Aarona.

< Masalimo 77 >