< Masalimo 68 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
En Psalmvisa Davids, till att föresjunga. Gud stånde upp, att hans fiender måga förströdde varda, och de honom hata, fly för honom.
2 Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
Fördrif dem, såsom en rök fördrifven varder; såsom vax försmälter för eld, så förgånge de ogudaktige för Gudi.
3 Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
Men de rättfärdige fröjde sig, och vare glade för Gudi, och fröjde sig af hjertat.
4 Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
Sjunger Gudi, lofsjunger hans Namne; görer honom väg, som sakta framfar; han heter Herren; och glädjens för honom.
5 Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
Den en fader är åt faderlösa, och en domare för enkom; han är Gud i sin helga boning;
6 Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
En Gud, som dem ensammom gifver huset fullt med barn; den der fångar utförer i rättom tid, och låter de affälliga blifva i det torra.
7 Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
Gud, då du utdrogst för ditt folk, då du gick i öknene; (Sela)
8 dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
Då bäfvade jorden, och himlarna dröpo för denna Guden i Sinai; för Gudi, som Israels Gud är.
9 Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
Men nu gifver du, Gud, ett nådeligit regn; och ditt arf, det torrt är, vederqvicker du;
10 Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
Att din djur måga bo deruti. Gud, du vederqvicker de elända med dine godhet.
11 Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
Herren gifver ordet, med en stor Evangelisters skara.
12 “Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
Konungarna för härarna äro med hvarannan vänner, och husäran utskifter rofvet.
13 Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
När I liggen i markene, så glimmar det såsom dufvovingar, hvilke såsom silfver och guld glittra.
14 Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
När den Allsmägtige allestäds ibland dem Konungar sätter, så varder klart, der mörkt är.
15 Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
Guds berg är ett fruktsamt berg, ett stort och fruktsamt berg.
16 Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
Hvi springen I, stor berg? Gud hafver lust till att bo på detta berget, och Herren blifver der ock evinnerliga.
17 Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
Guds vagn är mång tusende tusend. Herren är ibland dem på det helga Sinai.
18 Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
Du hafver farit upp i höjdena, och hafver fångat fängelset; du hafver undfått gåfvor för menniskorna; de affällige ock, att Herren Gud skall ändå likväl blifva der.
19 Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
Lofvad vare Herren dagliga. Gud lägger oss ena bördo uppå; men han hjelper oss ock. (Sela)
20 Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
Vi hafve en Gud, en Gud, den der hjelper, och Herran, Herran, den ifrå döden frälsar.
21 Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
Men Gud skall sönderslå hufvudet på sina fiendar, samt med deras hjessa, som blifva i deras synder.
22 Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
Dock säger Herren: Jag vill hemta somliga ibland de feta; utu hafsens djup vill jag somliga hemta.
23 Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
Derföre skall din fot uti fiendernas blod färgad varda, och dine hundar skola det slicka.
24 Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
Man ser, Gud, huru du går; huru du, min Gud och Konung, i helgedomenom går.
25 Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
De sångare gå framföre, der näst de spelmän, ibland pigor som slå på trummor.
26 Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
Lofver Herran Gud i församlingomen, för Israels brunn.
27 Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
Der är rådandes ibland dem den litsle BenJamin, Juda Förstar, med deras hopar, Sebulons Förstar, Naphthali Förstar.
28 Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
Din Gud hafver upprättat ditt rike, det stärk, Gud, i oss; ty det är ditt verk.
29 Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
För ditt tempels skull i Jerusalem, skola Konungar föra dig skänker.
30 Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
Straffa djuret i rören, oxahoparna ibland deras kalfvar, de der drifva för penningars skull. Han förströr de folk, som gerna örliga.
31 Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
De Förstar utur Egypten skola komma; Ethiopien skall utsträcka sina händer till Gud.
32 Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
I Konungariken på jordene, sjunger Gudi; lofsjunger Herranom. (Sela)
33 Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
Den der vistas i himmelen, allestädes af begynnelsen; si, han skall gifva sino dundre kraft.
34 Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
Gifver Gudi magten; hans härlighet är i Israel, och hans magt i skyn.
35 Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!
Gud är underlig i sinom helgedom; han är Israels Gud, han skall gifva folkena magt och kraft. Lofvad vare Gud.

< Masalimo 68 >