< Masalimo 68 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
For the chief musician; A psalm of David, a song. Let God arise; let his enemies be scattered; let those also who hate him flee before him.
2 Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
As smoke is driven away, so drive them away; as wax melts before the fire, so let the wicked perish in the presence of God.
3 Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
But let the righteous be glad; let them exult before God; may they rejoice and be happy.
4 Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
Sing to God! Sing praises to his name! Praise the one who rides through the plains of the Jordan River valley! Yahweh is his name! Rejoice before him!
5 Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
A father of the fatherless, a judge of the widows, is God in the holy place where he lives.
6 Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
God puts the lonely into families; he brings out the prisoners with singing; but the rebellious live in a parched land.
7 Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
God, when you went out before your people, when you marched through the wilderness, (Selah)
8 dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
The earth trembled; the heavens also dropped rain in God's presence, in the presence of God when he came to Sinai, in the presence of God, the God of Israel.
9 Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
You, God, sent a plentiful rain; you strengthened your inheritance when it was weary.
10 Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
Your people lived in it; You, God, gave from your goodness to the poor.
11 Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
The Lord gave the orders, and those who announced them were a great army.
12 “Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
Kings of armies flee, they flee, and the women waiting at home divide the plunder:
13 Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
doves covered with silver with wings of yellow gold. When some of you people stayed among the sheepfolds, why did you do this?
14 Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
The Almighty scattered kings there, it was as when it snowed on Mount Zalmon.
15 Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
A mighty mountain is the hill country of Bashan; a high mountain is the hill country of Bashan.
16 Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
Why do you look in envy, you high hill country, at the mountain which God desires for the place he will live? Indeed, Yahweh will live in it forever.
17 Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
The chariots of God are twenty thousand, thousands upon thousands; the Lord is among them in the holy place, as at Sinai.
18 Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
You have ascended on high; you have led away captives; you have received gifts from among men, even from those who fought against you, so that you, Yahweh God, might live there.
19 Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
Blessed be the Lord, who daily bears our burdens, the God who is our salvation. (Selah)
20 Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
Our God is a God who saves; Yahweh the Lord is the one who is able to rescue us from death.
21 Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
But God will strike through the heads of his enemies, through the hairy scalps of those who walk in offenses against him.
22 Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
The Lord said, “I will bring my enemies back from Bashan; I will bring them back from the depths of the sea
23 Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
so that you may crush your enemies, dipping your foot in blood, and so that the tongues of your dogs may have their share from your enemies.”
24 Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
They have seen your processions, God, the processions of my God, my King, into the holy place.
25 Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
The singers went first, the minstrels followed after, and in the middle were the unmarried girls playing tambourines.
26 Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
Bless God in the assemblies; praise Yahweh, you who are from the fountain of Israel.
27 Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
There is first Benjamin, the smallest tribe, then the leaders of Judah and their multitudes, the leaders of Zebulun and the leaders of Naphtali.
28 Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
Your God, Israel, has decreed your strength; reveal to us your power, God, as you have revealed it in times past.
29 Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
Reveal your power to us from your temple at Jerusalem, where kings bring gifts to you.
30 Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
Shout in battle against the wild beasts in the reeds, against the peoples, that multitude of bulls and calves. Humiliate them and make them bring you gifts; scatter the peoples who love to wage war.
31 Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
Princes will come out of Egypt; Cush will hurry to reach out with her hands to God.
32 Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
Sing to God, you kingdoms of the earth; (Selah) Sing praises to Yahweh.
33 Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
To him who rides on the heaven of heavens, which exist from ancient times; see, he lifts up his voice with power.
34 Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
Ascribe strength to God; his majesty is over Israel, and his strength is in the skies.
35 Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!
God, you are fearsome in your holy place; the God of Israel—he gives strength and power to his people. Blessed be God.

< Masalimo 68 >