< Masalimo 57 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
Aw Khawsa, nim qeen lah, nim qeen lah, kawtih nang awh ni ka hqingnaak ang thuk. Plawcinaak ang khum hlan dy nang hlak khuiawh thuk vang nyng.
2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
Kai aham ang cainaak ak soep sak Khawsa, sawsang soeih Khawsa venawh khy nyng.
3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
Anih ing khan nakawng tyi nawh kai ce ni hul hy, kai anik hquut khqek khqekkhqi ce toel hy.
4 Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
Kai taw samthyyn anglak li awh awm nyng saw; qamsak tlung anglakawh zaih nyng – ce thlangkhqi a ha taw ak hqat soeih zawzi na awm hy.
5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Aw Khawsa, khan poeng voelh dyna hak zoeksang qu lah; na boeimangnaak ve khawmdek boeih ak khan awh awm lah seh.
6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
Ka khaw ang awhnaak aham lawk zan law unawh kawboet doena ngam hqoeng nyng. Ka cehnaak lam awh lawk-kqawng co law hlai hy – a mimah ce lawk-kqawng awh tla lat uhy.
7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
Kam thin taw cak hy, Aw Bawipa kam thin ce cak hy; tingtoeng tum nawh laa sa vang.
8 Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
Ka hqingnaak, hqyng lah! Tingtoeng ingkaw qaw tingtoeng nang, hqyng lah! Kai taw mymcang hqit awh hqyng hawh kawng nyng.
9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
Pilnam thlang anglak li awh, Aw Bawipa, nang ce nim kyihcah vang. Thlanghqing lak awh nang ce laa na ni sa vang.
10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
Ikawtih, na lungnaak taw bau nawh, khan hak pha hy; na ypawmnaak ing khan hak pha hy.
11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Aw Khawsa, khan poe voelh dyna hak zoeksang qu lah; na boeimangnaak ve khawmdek boeih ak khan awh awm lah seh.

< Masalimo 57 >