< Masalimo 55 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
大衛的訓誨詩,交與伶長。用絲弦的樂器。 上帝啊,求你留心聽我的禱告, 不要隱藏不聽我的懇求!
2 mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
求你側耳聽我,應允我。 我哀歎不安,發聲唉哼,
3 chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
都因仇敵的聲音,惡人的欺壓; 因為他們將罪孽加在我身上,發怒氣逼迫我。
4 Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
我心在我裏面甚是疼痛; 死的驚惶臨到我身。
5 Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
恐懼戰兢歸到我身; 驚恐漫過了我。
6 Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
我說:但願我有翅膀像鴿子, 我就飛去,得享安息。
7 Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
我必遠遊, 宿在曠野。 (細拉)
8 Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
我必速速逃到避所, 脫離狂風暴雨。
9 Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
主啊,求你吞滅他們,變亂他們的舌頭! 因為我在城中見了強暴爭競的事。
10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
他們在城牆上晝夜繞行; 在城內也有罪孽和奸惡。
11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
邪惡在其中; 欺壓和詭詐不離街市。
12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
原來不是仇敵辱罵我, 若是仇敵,還可忍耐; 也不是恨我的人向我狂大, 若是恨我的人就必躲避他。
13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
不料是你;你原與我平等, 是我的同伴,是我知己的朋友!
14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
我們素常彼此談論,以為甘甜; 我們與群眾在上帝的殿中同行。
15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
願死亡忽然臨到他們! 願他們活活地下入陰間! 因為他們的住處,他們的心中,都是邪惡。 (Sheol h7585)
16 Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
至於我,我要求告上帝; 耶和華必拯救我。
17 Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
我要晚上、早晨、晌午哀聲悲歎; 他也必聽我的聲音。
18 Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
他救贖我命脫離攻擊我的人, 使我得享平安, 因為與我相爭的人甚多。
19 Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
那沒有更變、不敬畏上帝的人, 從太古常存的上帝必聽見而苦待他。
20 Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
他背了約, 伸手攻擊與他和好的人。
21 Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
他的口如奶油光滑, 他的心卻懷着爭戰; 他的話比油柔和, 其實是拔出來的刀。
22 Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
你要把你的重擔卸給耶和華, 他必撫養你; 他永不叫義人動搖。
23 Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.
上帝啊,你必使惡人下入滅亡的坑; 流人血、行詭詐的人必活不到半世, 但我要倚靠你。

< Masalimo 55 >