< Masalimo 49 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
To the Overseer. — By sons of Korah. A Psalm. Hear this, all ye peoples, Give ear, all ye inhabitants of the world.
2 anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
Both low and high, together rich and needy.
3 Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
My mouth speaketh wise things, And the meditations of my heart [are] things of understanding.
4 Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
I incline to a simile mine ear, I open with a harp my riddle:
5 Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
Why do I fear in days of evil? The iniquity of my supplanters doth compass me.
6 Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
Those trusting on their wealth, And in the multitude of their riches, Do shew themselves foolish.
7 Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
A brother doth no one at all ransom, He doth not give to God his atonement.
8 Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
And precious [is] the redemption of their soul, And it hath ceased — to the age.
9 kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
And still he liveth for ever, He seeth not the pit.
10 Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
For he seeth wise men die, Together the foolish and brutish perish, And have left to others their wealth.
11 Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
Their heart [is]: Their houses [are] to the age, Their tabernacles to all generations. They proclaimed their names over the lands.
12 Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
And man in honour doth not remain, He hath been like the beasts, they have been cut off.
13 Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
This their way [is] folly for them, And their posterity with their sayings are pleased. (Selah)
14 Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
As sheep for Sheol they have set themselves, Death doth afflict them, And the upright rule over them in the morning, And their form [is] for consumption. Sheol [is] a dwelling for him. (Sheol h7585)
15 Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
Only, God doth ransom my soul from the hand of Sheol, For He doth receive me. (Selah) (Sheol h7585)
16 Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
Fear not, when one maketh wealth, When the honour of his house is abundant,
17 Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
For at his death he receiveth nothing, His honour goeth not down after him.
18 Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
For his soul in his life he blesseth, (And they praise thee when thou dost well for thyself.)
19 iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
It cometh to the generation of his fathers, For ever they see not the light.
20 Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.
Man in honour, who understandest not, Hath been like the beasts, they have been cut off!

< Masalimo 49 >