< Masalimo 48 >

1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
Canto. Salmo de’ figliuoli di Core. Grande è l’Eterno e lodato altamente nella città dell’Iddio nostro, sul monte della sua santità.
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
Bello si erge, gioia di tutta la terra, il monte di Sion, dalle parti del settentrione, bella è la città del gran re.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
Nei palazzi d’essa Dio s’è fatto conoscere come un’alta fortezza.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
Poiché ecco, i re s’erano adunati, si avanzavano assieme.
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
Appena la videro, rimasero attoniti, smarriti, si misero in fuga,
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
un tremore li colse quivi, una doglia come di donna che partorisce.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
Col vento orientale tu spezzi le navi di Tarsis.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
Quel che avevamo udito l’abbiamo veduto nella città dell’Eterno degli eserciti, nella città del nostro Dio. Dio la renderà stabile in perpetuo. (Sela)
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
O Dio, noi abbiam meditato sulla tua benignità dentro al tuo tempio.
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
O Dio, qual è il tuo nome, tale è la tua lode fino all’estremità della terra; la tua destra è piena di giustizia.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
Si rallegri il monte di Sion, festeggino le figliuole di Giuda per i tuoi giudizi!
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Circuite Sion, giratele attorno, contatene le torri,
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
osservatene i bastioni, considerate i suoi palazzi, onde possiate parlarne alla futura generazione.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
Poiché questo Dio è il nostro Dio in sempiterno; egli sarà la nostra guida fino alla morte.

< Masalimo 48 >