< Masalimo 42 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi, kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.
Przewodnikowi chóru. Psalm pouczający dla synów Korego. Jak jeleń pragnie wód strumieni, tak moja dusza pragnie ciebie, Boże.
2 Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo. Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?
Moja dusza jest spragniona Boga, Boga żywego. Kiedy przyjdę i ukażę się przed obliczem Boga?
3 Misozi yanga yakhala chakudya changa usana ndi usiku, pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
Łzy stały się dla mnie chlebem we dnie i w nocy, gdy mówią do mnie co dzień: Gdzie jest twój Bóg?
4 Zinthu izi ndimazikumbukira pamene ndikukhuthula moyo wanga: momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu, kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko pakati pa anthu a pa chikondwerero.
Wylewam swą duszę, gdy wspominam, jak krocząc w tłumie, szedłem z nimi do domu Bożego wśród głosów radości i chwały, pośród świętującego tłumu.
5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Yembekezera Mulungu, pakuti ndidzamulambirabe, Mpulumutsi wanga ndi
Dlaczego się smucisz, moja duszo, i czemu się we mnie trwożysz? Zaufaj Bogu, bo jeszcze będę go wysławiał [za] jego zbawcze oblicze.
6 Mulungu wanga. Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga kotero ndidzakumbukira Inu kuchokera ku dziko la Yorodani, ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.
Mój Boże, smuci się we mnie moja dusza, dlatego wspominam cię z ziemi Jordanu i Hermonu, z góry Misar.
7 Madzi akuya akuyitana madzi akuya mu mkokomo wa mathithi anu; mafunde anu onse obwera mwamphamvu andimiza.
Przepaść przyzywa przepaść szumem twoich upustów; wszystkie twoje fale i nawałnice przewalają się nade mną.
8 Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake, nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane; pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.
Lecz we dnie PAN udzieli mi swego miłosierdzia, a w nocy [będzie] we mnie jego pieśń [i] moja modlitwa do Boga mego życia.
9 Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa, “Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?”
Powiem Bogu, mojej skale: Czemu o mnie zapomniałeś? Czemu chodzę smutny z powodu ucisku wroga?
10 Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo pamene adani anga akundinyoza, tsiku lonse akunena kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
Jak rana w moich kościach, tak mnie urągają moi wrogowie, gdy mówią do mnie każdego dnia: Gdzie jest twój Bóg?
11 Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.
Czemu się smucisz, moja duszo, i czemu się we mnie trwożysz? Zaufaj Bogu, bo jeszcze będę go wysławiał, [gdyż on jest] zbawieniem mego oblicza i moim Bogiem.

< Masalimo 42 >