< Masalimo 41 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
Blessed is he that considers the poor: the LORD will deliver him in time of trouble.
2 Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
The LORD will preserve him, and keep him alive; and he shall be blessed upon the earth: and you will not deliver him unto the will of his enemies.
3 Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
The LORD will strengthen him upon the bed of languishing: you will make all his bed in his sickness.
4 Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
I said, LORD, be merciful unto me: heal my soul; for I have sinned against you.
5 Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
Mine enemies speak evil of me, When shall he die, and his name perish?
6 Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
And if he comes to see me, he speaks vanity: his heart gathers iniquity to itself; when he goes abroad, he tells it.
7 Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
All that hate me whisper together against me: against me do they devise my hurt.
8 “Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
An evil disease, say they, cleaves fast unto him: and now that he lies he shall rise up no more.
9 Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
Yea, mine own familiar friend, in whom I trusted, which did eat of my bread, has lifted up his heel against me.
10 Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
But you, O LORD, be merciful unto me, and raise me up, that I may requite them.
11 Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
By this I know that you favour me, because mine enemy does not triumph over me.
12 Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
And as for me, you uphold me in mine integrity, and set me before your face for ever.
13 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.
Blessed be the LORD God of Israel from everlasting, and to everlasting. Amen, and Amen.

< Masalimo 41 >