< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
Davidi, cum immutavit vultum suum coram Achimelech, et dimisit eum et abiit. Benedicam Dominum in omni tempore: semper laus eius in ore meo.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
In Domino laudabitur anima mea: audiant mansueti, et lætentur.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Magnificate Dominum mecum: et exaltemus nomen eius in idipsum.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
Exquisivi Dominum, et exaudivit me: et ex omnibus tribulationibus meis eripuit me.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
Accedite ad eum, et illuminamini: et facies vestræ non confundentur.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
Iste pauper clamavit, et Dominus exaudivit eum: et de omnibus tribulationibus eius salvavit eum.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
Immittet angelus Domini in circuitu timentium eum: et eripiet eos.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Gustate, et videte quoniam suavis est Dominus: beatus vir, qui sperat in eo.
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
Timete Dominum omnes sancti eius: quoniam non est inopia timentibus eum.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
Divites eguerunt et esurierunt: inquirentes autem Dominum non minuentur omni bono.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Venite filii, audite me: timorem Domini docebo vos.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
Quis est homo qui vult vitam: diligit dies videre bonos?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Prohibe linguam tuam a malo: et labia tua ne loquantur dolum.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Diverte a malo, et fac bonum: inquire pacem, et persequere eam.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
Oculi Domini super iustos: et aures eius in preces eorum.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
Vultus autem Domini super facientes mala: ut perdat de terra memoriam eorum.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
Clamaverunt iusti, et Dominus exaudivit eos: et ex omnibus tribulationibus eorum liberavit eos.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
Iuxta est Dominus iis, qui tribulato sunt corde: et humiles spiritu salvabit.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Multæ tribulationes iustorum: et de omnibus his liberabit eos Dominus.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
Custodit Dominus omnia ossa eorum: unum ex his non conteretur.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Mors peccatorum pessima: et qui oderunt iustum delinquent.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
Redimet Dominus animas servorum suorum: et non delinquent omnes qui sperant in eo.

< Masalimo 34 >