< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
[A Psalm] of David, when he changed his behavior before Abimelech; who drove him away, and he departed. I will bless the LORD at all times: his praise [shall] continually [be] in my mouth.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
My soul shall make her boast in the LORD: the humble shall hear [of it] and be glad.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
O magnify the LORD with me, and let us exalt his name together.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
I sought the LORD, and he heard me, and delivered me from all my fears.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
They looked to him, and were lightened: and their faces were not ashamed.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
This poor man cried, and the LORD heard [him], and saved him out of all his troubles.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
The angel of the LORD encampeth around them that fear him, and delivereth them.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
O taste and see that the LORD [is] good: blessed [is] the man [that] trusteth in him.
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
O fear the LORD, ye his saints: for [there is] no want to them that fear him.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
The young lions do lack, and suffer hunger: but they that seek the LORD shall not want any good [thing].
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Come, ye children, hearken to me; I will teach you the fear of the LORD.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
What man [is he that] desireth life, [and] loveth [many] days, that he may see good?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Keep thy tongue from evil, and thy lips from speaking guile.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Depart from evil, and do good; seek peace, and pursue it.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
The eyes of the LORD [are] upon the righteous, and his ears [are open] to their cry.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
The face of the LORD [is] against them that do evil, to cut off the remembrance of them from the earth.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
[The righteous] cry, and the LORD heareth, and delivereth them out of all their troubles.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
The LORD [is] nigh to them that are of a broken heart; and saveth such as are of a contrite spirit.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Many [are] the afflictions of the righteous: but the LORD delivereth him out of them all.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
He keepeth all his bones: not one of them is broken.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Evil shall slay the wicked: and they that hate the righteous shall be desolate.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
The LORD redeemeth the soul of his servants: and none of them that trust in him shall be desolate.

< Masalimo 34 >