< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Ye iust men, haue fulli ioye in the Lord; presyng togidere bicometh riytful men.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Knouleche ye to the Lord in an harpe; synge ye to hym in a sautre of ten strengis.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Synge ye to hym a newe song; seie ye wel salm to hym in criyng.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
For the word of the Lord is riytful; and alle hise werkis ben in feithfulnesse.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
He loueth merci and doom; the erthe is ful of the merci of the Lord.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Heuenes ben maad stidfast bi the word of the Lord; and `al the vertu of tho bi the spirit of his mouth.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
And he gaderith togidere the watris of the see as in a bowge; and settith depe watris in tresours.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Al erthe drede the Lord; sotheli alle men enhabitynge the world ben mouyd of hym.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
For he seide, and thingis weren maad; he comaundide, and thingis weren maad of nouyt.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
The Lord distrieth the counsels of folkis, forsothe he repreueth the thouytis of puplis; and he repreueth the counsels of prynces.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
But the counsel of the Lord dwellith with outen ende; the thouytis of his herte dwellen in generacioun and into generacioun.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Blessid is the folk, whose Lord is his God; the puple which he chees into eritage to hym silf.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
The Lord bihelde fro heuene; he siy alle the sones of men.
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
Fro his dwellyng place maad redi bifor; he bihelde on alle men, that enhabiten the erthe.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
Which made syngulerli the soules of hem; which vndurstondith all the werkis of hem.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
A kyng is not sauyd bi myche vertu; and a giaunt schal not be sauyd in the mychilnesse of his vertu.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
An hors is false to helthe; forsothe he schal not be sauyd in the habundaunce, `ether plentee, of his vertu.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Lo! the iyen of the Lord ben on men dredynge hym; and in hem that hopen on his merci.
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
That he delyuere her soules fro deth; and feede hem in hungur.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Oure soule suffreth the Lord; for he is oure helpere and defendere.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
For oure herte schal be glad in him; and we schulen haue hope in his hooli name.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Lord, thi merci be maad on vs; as we hopiden in thee.

< Masalimo 33 >