< Masalimo 3 >

1 Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
Ein Psalm Davids, da er entwich vor seinem Sohne Absalom. Jehovah, wieviel sind meiner Dränger. Viele sind es, die wider mich aufstehen!
2 Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
Viele sprechen von meiner Seele: Keine Rettung hat er in Gott. (Selah)
3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
Doch Du, Jehovah, bist ein Schild für mich, meine Herrlichkeit, Du hebst mein Haupt empor.
4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
Mit meiner Stimme rufe ich zu Jehovah; und Er antwortet mir von dem Berg Seiner Heiligkeit. (Selah)
5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
Ich liege und schlafe; ich erwache; denn Jehovah erhält mich.
6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
Nicht fürchte ich mich vor Zehntausenden des Volks, die ringsum sich wider mich setzen.
7 Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
Mache Dich auf, Jehovah, rette mich, mein Gott! denn Du schlägst alle meine Feinde auf den Backen, Du zerbrichst der Ungerechten Zähne.
8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)
Bei Jehovah ist Heil! Dein Segen sei auf Deinem Volke. (Selah)

< Masalimo 3 >