< Masalimo 29 >

1 Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
大衛的詩。 上帝的眾子啊,你們要將榮耀、能力歸給耶和華, 歸給耶和華!
2 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
要將耶和華的名所當得的榮耀歸給他, 以聖潔的妝飾敬拜耶和華。
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
耶和華的聲音發在水上; 榮耀的上帝打雷, 耶和華打雷在大水之上。
4 Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
耶和華的聲音大有能力; 耶和華的聲音滿有威嚴。
5 Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
耶和華的聲音震破香柏樹; 耶和華震碎黎巴嫩的香柏樹。
6 Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
他也使之跳躍如牛犢, 使黎巴嫩和西連跳躍如野牛犢。
7 Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
耶和華的聲音使火焰分岔。
8 Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
耶和華的聲音震動曠野; 耶和華震動加低斯的曠野。
9 Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
耶和華的聲音驚動母鹿落胎, 樹木也脫落淨光。 凡在他殿中的,都稱說他的榮耀。
10 Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
洪水泛濫之時,耶和華坐着為王; 耶和華坐着為王,直到永遠。
11 Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.
耶和華必賜力量給他的百姓; 耶和華必賜平安的福給他的百姓。

< Masalimo 29 >