< Masalimo 27 >

1 Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
[Psalm lal David] LEUM GOD El kalem luk ac lango luk; Su nga ac fah sangeng se? LEUM GOD El pot ku nu ke moul luk, Su nga ac fah sangeng se?
2 Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
Ke mwet koluk elos tuku in lainyu ac suk in uniyuwi, Elos tukulkul ac ikori.
3 Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
Finne sie un mwet mweun tuku rauniyula, Nga fah tiana sangeng; Finne mwet lokoalok tuku lainyu, Nga fah lulalfongi na God.
4 Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
Nga siyuk sin LEUM GOD ke ma se, Ac ma sefanna nga lungsik: Tuh nga in muta in lohm sin LEUM GOD in moul luk nufon, In liye kasrpen wolana lal, Ac in siyuk ke koko lal.
5 Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
In pacl in ongoiya, El fah lisringyuyak; El fah karinginyu in Tempul lal Ac oru tuh nga in moulla fin sie eot fulat.
6 Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
Tuh nga fah kutangla mwet lokoalok su rauniyula. Nga fah orek kisa in lohm sel ke pusren engan lulap; Nga fah on, ac nga fah kaksakin LEUM GOD.
7 Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
Lohngyu, O LEUM GOD, ke nga pang nu sum! Pakomutuk ac topukyu!
8 Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
Ke kom fahk, “Fahsru ac alu nu sik,” Na nga topuk, “Aok, LEUM GOD, nga ac fahsrot.”
9 Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
Nikmet wikinkomla likiyu! Nikmet kasrkusrak sik; Nikmet supwala mwet kulansap lom liki kom. Kom nuna mwet kasru luk; Nikmet fahsr likiyu ku sisyula, O God, Mwet Lango luk.
10 Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
Sahp papa tumuk ac nina kiuk elos ku in sisyula, Tusruktu LEUM GOD El fah karinginyu.
11 Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
LEUM GOD, luti nu sik ma kom lungsum tuh nga in oru, Ac kolyu ke inkanek wo lom, Mweyen pus mwet lokoalok luk.
12 Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
Nikmet sisyula nu inpoun mwet lokoalok luk Su lainyu ke kas kikiap ac kas in aksangeng.
13 Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Nga etu tuh nga fah moul ac liye Woiyen LEUM GOD in moul se inge.
14 Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.
Lulalfongi in LEUM GOD. Lulalfongi, ac tia fuhleak. Lulalfongi na in LEUM GOD.

< Masalimo 27 >