< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Ikawtih, pilnam ing za qu unawh thlang boeih ing a hqawng a hqap mai awh aming hqum qu hy voei?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
Khawmdek sangpahrangkhqi ing Bawipa ingkaw Situi a syp thlang ce qaal na thawh sih uhy.
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
A mingmih a thiqui ce boet pe unawh taw, amik khawceh bynkhqi awm khawng pe valh u sih”, ti uhy.
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
Khan awh BOI na ak ngawi ce qaai nawh; Bawipa ing cekkhqi ce qaih am qin nak khqi hy.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Cekcoengawh a mingmih ce ak kawsonaak ing toel khqi nawh, ak kawtawknaak ing ly a lap sak khqi hy.
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
Kamah qoe ing ka tlang ciim Zion awh ka sangpahrang ce ngawih sak hawh nyng”, tinawh kqawn hy.
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
Bawipa ak awipeek ce khypyi kawng. “Nang taw ka capa na awm hyk ti; tuhngawi awhkawng na capa na awm nyng” ni tina hy.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Thoeh law lah cawhtaw pilnam ce qo na ni pe kawng, khawmdek a dytnaak dy na koena awm kaw.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Thicung ing a mingmih ce nang ing uk khqi kawp ti, dek-am ami deep kqek kqek amyihna cekkhqi ce deep khqi kqek kqek kawp ti.
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Cedawngawh nangmih sangpahrangkhqi, cyi unawh taw, Aw nangmih khawmdek ukkungkhqi ngaihtaak ing awm hlah uh.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Kqih doena Bawipa bi ce bi unawh awmhly doena thyn lah uh.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Cakpa ce mawk lah uh, cekaa awhtaw ak kaw so kawmsaw na lam awh plawci hau kawp ti.

< Masalimo 2 >