< Masalimo 16 >

1 Mikitamu ya Davide. Ndisungeni Inu Mulungu, pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
A Precious Psalm of David. Preserve me, O GOD, for I have sought refuge in thee.
2 Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga; popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
Thou hast said unto Yahweh, My Lord, art thou! My goodness, mounteth not unto thee.
3 Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko, amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
It belongeth unto the holy ones, whom, in his own land, Yahweh, ennobleth, In whom is all his delight
4 Anthu amene amathamangira kwa milungu ina mavuto awo adzachulukadi. Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
They multiply their idols—another, have they purchased! I will not pour out their drink-offerings of blood, nor will I take up their names on my lips.
5 Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa; mwateteza kolimba gawo langa.
Yahweh, is mine allotted portion and my cup, Thou, art maintaining my lot.
6 Malire a malo anga akhala pabwino; ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
The lines, have fallen unto me, in pleasant places, Verily an inheritance that delighteth me.
7 Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu; ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
I will bless Yahweh, who hath counselled me, —Surely, by night, shall mine impulses admonish me.
8 Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
I have set Yahweh before me continually, because he is on my right hand, I shall not be shaken!
9 Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera; thupi langanso lidzakhala pabwino,
Therefore, hath my heart rejoiced, and mine honour exulted, Yea, my flesh, shall settle down securely;
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol h7585)
For thou wilt not abandon my soul to hades, neither wilt thou suffer thy man of lovingkindness, to see corruption: (Sheol h7585)
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo; mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu, ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.
Thou wilt cause me to know, the path of life, —Fulness of joys before thee, Pleasures at thy right hand evermore.

< Masalimo 16 >