< Masalimo 139 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
For the Chief Musician. A Psalm by David. LORD, you have searched me, and you know me.
2 Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
You know my sitting down and my rising up. You perceive my thoughts from afar.
3 Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
You search out my path and my lying down, and are acquainted with all my ways.
4 Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
For there is not a word on my tongue, but behold, LORD, you know it altogether.
5 Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
You hem me in behind and before. You laid your hand on me.
6 Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
This knowledge is beyond me. It’s lofty. I can’t attain it.
7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
Where could I go from your Spirit? Or where could I flee from your presence?
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
If I ascend up into heaven, you are there. If I make my bed in Sheol, behold, you are there! (Sheol h7585)
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
If I take the wings of the dawn, and settle in the uttermost parts of the sea,
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
even there your hand will lead me, and your right hand will hold me.
11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
If I say, “Surely the darkness will overwhelm me. The light around me will be night,”
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
even the darkness doesn’t hide from you, but the night shines as the day. The darkness is like light to you.
13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
For you formed my inmost being. You knit me together in my mother’s womb.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
I will give thanks to you, for I am fearfully and wonderfully made. Your works are wonderful. My soul knows that very well.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
My frame wasn’t hidden from you, when I was made in secret, woven together in the depths of the earth.
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
Your eyes saw my body. In your book they were all written, the days that were ordained for me, when as yet there were none of them.
17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
How precious to me are your thoughts, God! How vast is their sum!
18 Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
If I would count them, they are more in number than the sand. When I wake up, I am still with you.
19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
If only you, God, would kill the wicked. Get away from me, you bloodthirsty men!
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
For they speak against you wickedly. Your enemies take your name in vain.
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
LORD, don’t I hate those who hate you? Am I not grieved with those who rise up against you?
22 Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
I hate them with perfect hatred. They have become my enemies.
23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
Search me, God, and know my heart. Try me, and know my thoughts.
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.
See if there is any wicked way in me, and lead me in the everlasting way.

< Masalimo 139 >