< Masalimo 135 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Praise Yahweh. Praise the name of Yahweh. Praise him, you servants of Yahweh,
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
you who stand in Yahweh's house, in the courtyards of the house of our God.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Praise Yahweh, for he is good; sing praises to his name, for it is pleasant to do so.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
For Yahweh has chosen Jacob for himself, Israel as his possession.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
I know that Yahweh is great, that our Lord is above all gods.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
Whatever Yahweh desires, he does in heaven, on earth, in the seas and all the ocean depths.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
He brings the clouds from far away, making lightning bolts accompany the rain and bringing the wind out of his storehouse.
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
He killed the firstborn of Egypt, both of man and animals.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
He sent signs and wonders into your midst, Egypt, against Pharaoh and all his servants.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
He attacked many nations and killed mighty kings,
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Sihon king of the Amorites and Og king of Bashan and all the kingdoms of Canaan.
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
He gave us their land as an inheritance, an inheritance to Israel his people.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Your name, Yahweh, endures forever; your renown, Yahweh, endures throughout all generations.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
For Yahweh defends his people and has compassion on his servants.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
The nations' idols are silver and gold, the work of men's hands.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
Those idols have mouths, but they do not speak; they have eyes, but they do not see;
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
they have ears, but they do not hear, nor is there breath in their mouths.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Those who make them are like them, as is everyone who trusts in them.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Descendants of Israel, bless Yahweh; descendants of Aaron, bless Yahweh.
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
Descendants of Levi, bless Yahweh; you who honor Yahweh, bless Yahweh.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Blessed be Yahweh in Zion, he who lives in Jerusalem. Praise Yahweh.

< Masalimo 135 >