< Masalimo 135 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Let the Lord be praised. O you servants of the Lord, give praise to the name of the Lord.
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
You who are in the house of the Lord, and in the open spaces of the house of our God,
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Give praise to Jah, for he is good: make melody to his name, for it is pleasing.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
For the Lord has taken Jacob for himself, and Israel for his property.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
I know that the Lord is great, and that our Lord is greater than all other gods.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
The Lord has done whatever was pleasing to him, in heaven, and on the earth, in the seas and in all the deep waters.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
He makes the mists go up from the ends of the earth; he makes thunder-flames for the rain; he sends out the winds from his store-houses.
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
He put to death the first-fruits of Egypt, of man and of beast.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
He sent signs and wonders among you, O Egypt, on Pharaoh, and on all his servants.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
He overcame great nations, and put strong kings to death;
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Sihon, king of the Amorites, and Og, king of Bashan, and all the kingdoms of Canaan;
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
And gave their land for a heritage, even for a heritage to Israel his people.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
O Lord, your name is eternal; and the memory of you will have no end.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
For the Lord will be judge of his people's cause; his feelings will be changed to his servants.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
The images of the nations are silver and gold, the work of men's hands.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
They have mouths, but no voice, they have eyes, but they do not see;
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
They have ears, but no hearing; and there is no breath in their mouths.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Those who make them are like them; and so is everyone who puts his hope in them.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Give praise to the Lord, O children of Israel: give praise to the Lord, O sons of Aaron:
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
Give praise to the Lord, O sons of Levi: let all the worshippers of the Lord give him praise.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Praise be to the Lord out of Zion, even to the Lord whose house is in Jerusalem, Let the Lord be praised.

< Masalimo 135 >