< Masalimo 120 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
[A Song of Ascents.] In my distress, I cried to the LORD. He answered me.
2 Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
Deliver my soul, LORD, from lying lips, from a deceitful tongue.
3 Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
What will be given to you, and what will be done more to you, you deceitful tongue?
4 Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
Sharp arrows of the mighty, with coals of juniper.
5 Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
Woe is me, that I live in Meshech, that I dwell among the tents of Kedar.
6 Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
My soul has had her dwelling too long with him who hates peace.
7 Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.
I am for peace, but when I speak, they are for war.

< Masalimo 120 >