< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
BEATI coloro che sono intieri di via, Che camminano nella Legge del Signore.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Beati coloro che guardano le sue testimonianze, Che lo cercano con tutto il cuore;
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
[I quali] eziandio non operano iniquità; [Anzi] camminano nelle sue vie.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Tu hai ordinato che i tuoi comandamenti Sieno strettamente osservati.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Oh! sieno pure addirizzate le mie vie, Per osservare i tuoi statuti.
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Allora io non sarò svergognato, Quando io riguarderò a tutti i tuoi comandamenti.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Io ti celebrerò con dirittura di cuore, Quando io avrò imparate le leggi della tua giustizia.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Io osserverò i tuoi statuti; Non abbandonarmi del tutto.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Come renderà il fanciullo la sua via pura? Prendendo guardia [ad essa] secondo la tua parola.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Io ti ho cercato con tutto il mio cuore; Non lasciarmi deviar da' tuoi comandamenti.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Io ho riposta la tua parola nel mio cuore; Acciocchè io non pecchi contro a te.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Tu [sei] benedetto, o Signore; Insegnami i tuoi statuti.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Io ho colle mie labbra raccontate Tutte le leggi della tua bocca.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Io gioisco nella via delle tue testimonianze, Come per tutte le ricchezze [del mondo].
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Io ragiono de' tuoi comandamenti, E riguardo a' tuoi sentieri.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Io mi diletto ne' tuoi statuti; Io non dimenticherò le tue parole.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Fa' del bene al tuo servitore, Ed io viverò, ed osserverò la tua parola.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Apri gli occhi miei, ed io riguarderò Le maraviglie della tua Legge.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Io [son] forestiere in terra; Non nascondermi i tuoi comandamenti.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
L'anima mia si stritola di affezione Alle tue leggi in ogni tempo.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Tu sgridi i superbi maledetti Che deviano da' tuoi comandamenti.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Togli d'addosso a me il vituperio e lo sprezzo; Perciocchè io ho guardate le tue testimonianze.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Eziandio, [mentre] i principi sedevano, e ragionavano contro a me, Il tuo servitore ha meditato ne' tuoi statuti.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Ed anche le tue testimonianze [sono] i miei diletti [Ed] i miei consiglieri.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
L'anima mia è attaccata alla polvere; Vivificami secondo la tua parola.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Io [ti] ho narrate le mie vie, e tu mi hai risposto; Insegnami i tuoi statuti.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Fammi intender la via de' tuoi comandamenti, Ed io ragionerò delle tue maraviglie.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
L'anima mia stilla di cordoglio; Sollevami secondo le tue parole.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Rimuovi da me la via della menzogna; E fammi dono della tua Legge.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Io ho scelta la via della verità; Io [mi] son proposte le tue leggi.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Io mi son tenuto alle tue testimonianze; Signore, non lasciar che io sia confuso.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Correrò nella via de' tuoi comandamenti, Quando tu mi avrai allargato il cuore.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Insegnami, Signore, la via de' tuoi statuti; Ed io la guarderò [infino] al fine.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Dammi intelletto, ed io guarderò la tua Legge; E l'osserverò con tutto il cuore.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Conducimi per lo sentiero de' tuoi comandamenti; Perciocchè io mi diletto in esso.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Inchina il mio cuore alle tue testimonianze, E non a cupidigia.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Storna gli occhi miei, che non riguardino a vanità; Vivificami nelle tue vie.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Attieni la tua parola al tuo servitore, Il quale [è tutto] intento al tuo timore.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Rimuovi [da me] il mio vituperio, del quale io temo; Perciocchè le tue leggi [son] buone.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Ecco, io desidero affettuosamente i tuoi comandamenti; Vivificami nella tua giustizia.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Ed avvenganmi le tue benignità, o Signore; [E] la tua salute, secondo la tua parola.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Ed io risponderò a colui che mi fa vituperio; Perciocchè io mi confido nella tua parola.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
E non ritrarmi del tutto dalla bocca la parola della verità; Perciocchè io spero nelle tue leggi.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Ed io osserverò la tua Legge del continuo, In sempiterno.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
E camminerò al largo; Perciocchè io ho ricercati i tuoi comandamenti.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
E parlerò delle tue testimonianze davanti ai re, E non sarò svergognato.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
E mi diletterò ne' tuoi comandamenti, I quali io amo.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Ed alzerò le palme delle mie mani a' tuoi comandamenti, i quali io amo; E mediterò ne' tuoi statuti.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Ricordati della parola [detta] al tuo servitore, Sopra la quale tu mi hai fatto sperare.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Questa [è] la mia consolazione nella mia afflizione, Che la tua parola mi ha vivificato.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
I superbi mi hanno grandemente schernito; [Ma] io non mi sono stornato dalla tua Legge.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Signore, io mi son ricordato de' tuoi giudicii ab antico; E mi son consolato.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Tremito mi occupa, per gli empi Che abbandonano la tua Legge.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
I tuoi statuti sono stati i miei cantici Nella dimora de' miei pellegrinaggi.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
O Signore, di notte io mi son ricordato del tuo Nome, Ed ho osservata la tua Legge.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Questo mi è avvenuto, Perciocchè io ho guardati i tuoi comandamenti.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Il Signore [è] la mia parte; Io ho detto di osservare le tue parole.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Io ti ho supplicato con tutto il cuore; Abbi pietà di me, secondo la tua parola.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Io ho fatta ragione delle mie vie; Ed ho rivolti i miei piedi alle tue testimonianze.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Io mi sono affrettato, e non mi sono indugiato D'osservare i tuoi comandamenti.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Schiere d'empi mi hanno predato; [Ma però] non ho dimenticata la tua Legge.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Io mi levo a mezzanotte, per celebrarti, Per le leggi della tua giustizia.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Io [son] compagno di tutti quelli che ti temono, Ed osservano i tuoi comandamenti.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Signore, la terra è piena della tua benignità; Insegnami i tuoi statuti.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Signore, tu hai usata beneficenza inverso il tuo servitore, Secondo la tua parola.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Insegnami buon senno ed intendimento; Perciocchè io credo a' tuoi comandamenti.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Avanti che io fossi afflitto, io andava errando; Ma ora osservo la tua parola.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Tu [sei] buono e benefattore; Insegnami i tuoi statuti.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
I superbi hanno acconciate delle bugie contro a me; [Ma] io con tutto il cuore guarderò i tuoi comandamenti.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Il cuor loro è condenso come grasso; [Ma] io mi diletto nella tua Legge.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Egli [è stato] buono per me, che io sono stato afflitto; Acciocchè io impari i tuoi statuti.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
La Legge della tua bocca mi [è] migliore Che le migliaia d'oro e d'argento.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Le tue mani mi hanno fatto e formato; Dammi intelletto, ed io imparerò i tuoi comandamenti.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Quelli che ti temono mi vedranno, e si rallegreranno; Perciocchè io ho sperato nella tua parola.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
O Signore, io so che i tuoi giudicii [non sono altro che] giustizia; E [che ciò che] mi hai afflitto [è stato] fedeltà.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Deh! [sia] la tua benignità per consolarmi, Secondo la tua parola, [detta] al tuo servitore.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Avvenganmi le tue misericordie, acciocchè io viva; Perciocchè la tua Legge [è] ogni mio diletto.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Sien confusi i superbi, perciocchè a torto mi sovvertono; [Ma] io medito ne' tuoi comandamenti.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Rivolgansi a me quelli che ti temono. E quelli che conoscono le tue testimonianze.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Sia il mio cuore intiero ne' tuoi statuti; Acciocchè io non sia confuso.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
L'anima mia vien meno dietro alla tua salute; Io spero nella tua parola.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Gli occhi miei vengono meno dietro alla tua parola, Dicendo: Quando mi consolerai tu?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Perciocchè io son divenuto come un otro al fumo; E [pur] non ho dimenticati i tuoi statuti.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Quanti [hanno da essere] i giorni del tuo servitore? Quando farai giudicio sopra quelli che mi perseguitano?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
I superbi mi hanno cavate delle fosse; Il che non [è] secondo la tua Legge.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Tutti i tuoi comandamenti [son] verità; Essi mi perseguitano a torto; soccorrimi.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Mi hanno pressochè distrutto ed atterrato; [Ma] io non ho abbandonati i tuoi comandamenti.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Vivificami secondo la tua benignità, Ed io osserverò la testimonianza della tua bocca.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
O Signore, la tua parola [è] in eterno; Ella è stabile ne' cieli.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
La tua verità [è] per ogni età; Tu hai stabilita la terra, ed ella sta ferma.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
[Il cielo e la terra] stanno anche oggi fermi, per li tuoi ordini, Perciocchè ogni cosa [è] al tuo servigio.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Se la tua Legge [non fosse stata] ogni mio diletto, Io già sarei perito nella mia afflizione.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Giammai non dimenticherò i tuoi comandamenti; Perciocchè per essi tu mi hai vivificato.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Io [son] tuo, salvami; Perciocchè io ho ricercati i tuoi comandamenti.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Gli empi mi hanno atteso, per farmi perire; [Ma] io ho considerate le tue testimonianze.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Io ho veduto che tutte le cose le più perfette hanno fine; Ma il tuo comandamento [è] d'una grandissima distesa.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Oh! quanto amo la tua Legge! Ella [è] la mia meditazione di tutti i giorni.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
[Per] li tuoi comandamenti tu mi rendi più savio che i miei nemici; Perciocchè [quelli] in perpetuo [sono] miei.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Io son più intendente che tutti i miei dottori; Perciocchè le tue testimonianze [son] la mia meditazione.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Io son più avveduto che i vecchi; Perciocchè io ho guardati i tuoi comandamenti.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Io ho rattenuti i miei piedi da ogni sentiero malvagio; Acciocchè io osservi la tua parola.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Io non mi sono stornato dalle tue leggi; Perciocchè tu mi hai ammaestrato.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Oh! quanto son dolci le tue parole al mio palato! [Son più dolci] che miele alla mia bocca.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Io son divenuto avveduto per li tuoi comandamenti; Perciò, odio ogni sentiero di falsità.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
La tua parola [è] una lampana al mio piè, Ed un lume al mio sentiero.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Io ho giurato, e l'atterrò, Di osservare le leggi della tua giustizia.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Io son sommamente afflitto; O Signore, vivificami secondo la tua parola.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Deh! Signore, gradisci le offerte volontarie della mia bocca, Ed insegnami le tue leggi.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Io ho l'anima mia del continuo in palma di mano; E pur non ho dimenticata la tua Legge.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Gli empi mi hanno tesi de' lacci; E pur non mi sono sviato da' tuoi comandamenti.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Le tue testimonianze [son] la mia eredità in perpetuo; Perciocchè esse [son] la letizia del mio cuore.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Io ho inchinato il mio cuore a mettere in opera i tuoi statuti, In perpetuo, infino al fine.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Io odio i discorsi; Ma amo la tua Legge.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Tu [sei] il mio nascondimento, ed il mio scudo; Io spero nella tua parola.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Ritraetevi da me, maligni; Ed io guarderò i comandamenti del mio Dio.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Sostienmi, secondo la tua parola, ed io viverò; E non rendermi confuso della mia speranza.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Confortami, ed io sarò salvato; E riguarderò del continuo a' tuoi statuti.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Tu calpesti tutti quelli che si sviano da' tuoi statuti; Perciocchè la lor frode [è] una cosa falsa.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Tu riduci al niente tutti gli empi della terra, [come] schiume; Perciò io amo le tue testimonianze.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
La mia carne si raccapriccia tutta per lo spavento di te; Ed io temo de' tuoi giudicii.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Io ho fatto ciò che è diritto e giusto; Non abbandonarmi a quelli che mi oppressano.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Da' sicurtà per lo tuo servitore in bene, [E] non [lasciar] che i superbi mi oppressino.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Gli occhi miei vengono meno dietro alla tua salute, Ed alla parola della tua giustizia.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Opera inverso il tuo servitore secondo la tua benignità, Ed insegnami i tuoi statuti.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Io [son] tuo servitore; dammi intelletto; Acciocchè io possa conoscere le tue testimonianze.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
[Egli è] tempo che il Signore operi; Essi hanno annullata la tua Legge.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Perciò io amo i tuoi comandamenti più che oro; Anzi più che oro finissimo.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Perciò approvo, come diritti, tutti i tuoi comandamenti intorno ad ogni cosa; [Ed] odio ogni sentiero di menzogna.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Le tue testimonianze [son] cose maravigliose; Perciò l'anima mia le ha guardate.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
La dichiarazione delle tue parole allumina, [E] dà intelletto a' semplici.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Io ho aperta la bocca, ed ho ansato; Perciocchè io ho bramati i tuoi comandamenti.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Riguarda a me, ed abbi pietà di me, Secondo ch'è ragionevole [di fare] inverso quelli che amano il tuo Nome.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Ferma i miei passi nella tua parola; E non [lasciare] che alcuna iniquità signoreggi sopra me.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Riscuotimi dall'oppressione degli uomini; Ed io osserverò i tuoi comandamenti.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Fa' rilucere il tuo volto sopra il tuo servitore;
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Ed insegnami i tuoi statuti. Ruscelli d'acque mi scendono giù dagli occhi; Perciocchè la tua Legge non è osservata.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
O Signore, tu [sei] giusto, E i tuoi giudicii [son] diritti.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Tu hai strettamente comandata la giustizia, E la verità delle tue testimonianze.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Il mio zelo mi consuma; Perciocchè i miei nemici hanno dimenticate le tue parole.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
La tua parola [è] sommamente purgata; E però il tuo servitore l'ama.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Io [son] piccolo e sprezzato; [Ma però] non ho dimenticati i tuoi comandamenti.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
La tua giustizia [è] una giustizia eterna, E la tua Legge [è] verità.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Tribolazione e distretta mi hanno colto; [Ma] i tuoi comandamenti [sono] i miei diletti.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Le tue testimonianze sono una giustizia eterna; Dammi intelletto, ed io viverò.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Io ho gridato con tutto il cuore; rispondimi, Signore; [Ed] io guarderò i tuoi statuti.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Io ti ho invocato; salvami, Ed io osserverò le tue testimonianze.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Io mi son fatto avanti all'alba, ed ho gridato; Io ho sperato nella tua parola.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Gli occhi miei prevengono le vigilie [della notte]. Per meditar nella tua parola.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Ascolta la mia voce, secondo la tua benignità; O Signore, vivificami, secondo che tu hai ordinato.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Quelli che vanno dietro a scelleratezza, E si sono allontanati dalla tua Legge, si sono accostati [a me].
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
O Signore, tu [sei] vicino; E tutti i tuoi comandamenti [son] verità.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Gran tempo è che io so [questo] delle tue testimonianze, Che tu le hai stabilite in eterno.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Riguarda alla mia afflizione, e tramme[ne] fuori; Perciocchè io non ho dimenticata la tua Legge.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Dibatti la mia lite, e riscuotimi; Vivificami, secondo la tua parola.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
La salute [è] lungi dagli empi; Perciocchè non ricercano i tuoi statuti.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Le tue misericordie [son] grandi, Signore; Vivificami secondo ciò che hai ordinato.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
I miei persecutori ed i miei nemici [son] molti; [Ma] io non mi sono deviato dalle tue testimonianze.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Io ho veduti i disleali, e ne ho sentita gran noia; Perciocchè non osservano la tua parola.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Vedi quanto amo i tuoi comandamenti! Signore, vivificami, secondo la tua benignità.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
La somma della tua parola [è] verità; E tutte le leggi della tua giustizia [sono] in eterno.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
I principi m'hanno perseguitato senza cagione; Ma il mio cuore ha spavento della tua parola.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Io mi rallegro per la tua parola, Come una persona che avesse trovate grandi spoglie.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Io odio ed abbomino la menzogna; [Ma] io amo la tua Legge.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Io ti lodo sette volte il dì, Per li giudicii della tua giustizia.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Quelli che amano la tua Legge godono di molta pace; E non [vi è] alcuno intoppo per loro.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Signore, io ho sperato nella tua salute; Ed ho messi in opera i tuoi comandamenti.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
L'anima mia ha osservate le tue testimonianze; Ed io le ho grandemente amate.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Io ho osservati i tuoi comandamenti, e le tue testimonianze; Perciocchè tutte le mie vie [sono] nel tuo cospetto.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Pervenga il mio grido al tuo cospetto, o Signore; Dammi intelletto, secondo la tua parola.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Venga la mia supplicazione in tua presenza; Riscuotimi, secondo la tua parola.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Le mie labbra sgorgheranno lode, Quando tu mi avrai insegnati i tuoi statuti.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
La mia lingua ragionerà della tua parola; Perciocchè tutti i tuoi comandamenti [son] giustizia.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Siami in aiuto la tua mano; Perciocchè io ho eletti i tuoi comandamenti.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Signore, io ho desiderata la tua salute; E la tua Legge [è] ogni mio diletto.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Viva l'anima mia, ed ella ti loderà; E soccorranmi i tuoi ordinamenti.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Io vo errando, come una pecora smarrita; cerca il tuo servitore; Perciocchè io non ho dimenticati i tuoi comandamenti.

< Masalimo 119 >