< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Heureux ceux dont la voie est innocente, qui marchent selon la loi de l'Éternel!
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Heureux ceux qui observent ses ordonnances, le cherchent de tout leur cœur,
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
ne commettent point le mal, et marchent dans ses voies!
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Tu as prescrit tes commandements, pour qu'on les garde avec soin!
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
O! si mes voies étaient dirigées vers l'observation de tes commandements!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Alors je ne serais pas confus, en considérant tous tes préceptes.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Je te louerai d'un cœur sincère, en apprenant tes justes lois.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Je veux garder tes commandements: ne me laisse pas trop dans l'abandonnement! Beth.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Comment un jeune homme rendra-t-il sa voie pure? C'est en la surveillant d'après ta parole.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Je te cherche de tout mon cœur: fais que je ne m'écarte pas de tes commandements!
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Je serre ta parole dans mon cœur, afin de ne point pécher contre toi.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Sois béni, ô Éternel! enseigne-moi tes décrets!
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
De mes lèvres j'énumère toutes les lois sorties de ta bouche.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
La voie que tracent tes préceptes, me donne autant de joie que tous les trésors.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Je veux méditer tes commandements, et avoir les yeux sur tes sentiers.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Je fais mes délices de tes décrets, et je n'oublie point ta parole. Guimel.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Fais du bien à ton serviteur, pour que je vive, et que j'observe ta parole!
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Dessille mes yeux, pour que je découvre les merveilles cachées dans ta loi!
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Je suis un étranger sur la terre: ne me cèle pas tes commandements!
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Mon âme se consume à désirer tes lois en tout temps.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Tu gourmandes les superbes, hommes maudits, qui s'écartent de tes commandements.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Décharge-moi de l'opprobre et du mépris, car j'observe tes ordonnances!
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Des princes mêmes se sont concertés contre moi: ton serviteur médite tes statuts;
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
tes ordres sont aussi mes délices et mes conseillers. Daleth.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Mon âme gît dans la poudre: rends-moi la vie selon ta promesse!
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Je te raconte mes voies, et tu m'exauces: enseigne-moi tes ordonnances!
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Fais-moi découvrir la voie tracée par tes lois, et je veux approfondir tes merveilles!
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Mon âme pleure de chagrin: relève-moi selon ta promesse!
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Tiens à distance de moi le chemin du mensonge, et accorde-moi la faveur de [connaître] ta loi!
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Je choisis le chemin de la vérité, et je me propose tes jugements.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Je m'attache à tes ordonnances: Éternel, ne me rends pas confus!
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Je courrai dans la voie de tes commandements, car tu ouvres mon cœur. Hé.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Éternel, indique-moi la voie de tes statuts, afin que je la tienne jusques au bout!
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Donne-moi l'intelligence, pour que je garde ta loi, et que je l'observe de tout mon cœur!
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Fais-moi suivre le sentier de tes préceptes, car j'en fais mes délices!
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Incline mon cœur vers tes préceptes, et non vers l'amour du gain!
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Détourne mes yeux de regarder ce qui est vain, anime-moi sur tes sentiers!
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Envers ton serviteur remplis ta promesse, qui fut faite à la crainte qu'on a de toi!
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Tiens loin de moi l'opprobre que je redoute, car tes jugements sont pleins de bonté!
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Voici, je porte mes désirs vers tes commandements, fais-moi vivre dans ta justice! Vav.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Et que tes grâces arrivent jusqu'à moi, Éternel, ton secours, selon ta promesse!
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
afin que je puisse répondre à celui qui m'outrage; car je me confie en ta promesse.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
N'ôte jamais de ma bouche le langage de la vérité! car je suis dans l'attente de tes jugements.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Et j'observerai ta loi constamment, à jamais, perpétuellement;
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
et je marcherai dans une voie spacieuse, car je cherche tes commandements.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Et je parlerai de ta loi en présence des rois, et je n'aurai point de honte.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Et je ferai mes délices de tes commandements, que j'aime,
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
et je lèverai mes mains vers tes commandements que j'aime et je méditerai tes statuts. Zaïn.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Souviens-toi de ta promesse à ton serviteur, puisque tu m'as donné l'espérance!
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Voici ma consolation dans ma misère, c'est que ta promesse me redonne la vie.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Des superbes me tournent en grande dérision; de ta loi je ne dévie point.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Je me rappelle tes jugements de jadis, Éternel, et je me console.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Un bouillant transport me saisit à la vue des impies, qui abandonnent ta loi.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Tes décrets me suggèrent des cantiques, dans le lieu de mon exil.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
La nuit je pense à ton nom, Éternel, et j'observe ta loi.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Voici ce qui m'est propre, c'est que je garde tes commandements. Cheth.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Mon partage, ô Éternel, je le dis, c'est de garder tes paroles.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Je cherche ta faveur de toute mon âme: sois-moi propice selon ta promesse!
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Je suis circonspect dans mes voies, et je retourne mes pas vers tes commandements.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Je me hâte, et ne diffère point d'observer tes commandements.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Les pièges des impies m'enveloppent; je n'oublie point ta loi.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Au milieu de la nuit, je me lève pour te louer des jugements de ta justice.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Je me lie avec tous ceux qui te craignent, et observent tes commandements.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
La terre, ô Éternel, est pleine de ta grâce: enseigne-moi tes ordonnances! Theth.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Tu fais du bien à ton serviteur, Éternel, selon ta promesse.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Enseigne-moi la bonne science et la connaissance! car je crois en tes commandements.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Avant mon humiliation, je m'égarais; mais maintenant je prends garde à ta parole.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Tu es bon et bienfaisant; enseigne-moi tes statuts!
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Des superbes contre moi ourdissent l'astuce; moi, de tout mon cœur j'observe tes commandements.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Leur cœur a l'insensibilité de la graisse, moi, je fais mes délices de ta loi.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Il m'est utile d'avoir été humilié, pour devenir docile à tes préceptes.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
La loi qui sort de ta bouche a plus de prix pour moi que des milliers d'or et d'argent. Jod.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Tes mains m'ont créé, m'ont formé; donne-moi l'intelligence, pour apprendre tes statuts!
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Ceux qui te craignent, me verront et se réjouiront, car j'espère dans tes promesses.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Je sais, Éternel, que tes jugements sont justes, et que tu m'as affligé en demeurant fidèle.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
O que ta grâce soit ma consolation, selon ta promesse à ton serviteur!
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Envoie-moi ta miséricorde, pour que j'aie la vie! car ta loi fait mes délices.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Que les superbes soient confondus, car ils m'accablent gratuitement! pour moi, je médite tes commandements.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Qu'ils reviennent à moi ceux qui te craignent, et ceux qui connaissent tes commandements!
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Que mon cœur soit tout à tes ordonnances, afin que je ne sois pas confondu! Caph.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Mon âme languit après ton salut; je compte sur ta promesse.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Mes yeux s'éteignent dans l'attente de ta promesse, je dis: Quand me consoleras-tu?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Car je suis comme une outre fumée; je n'oublie point tes commandements.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Quel est le nombre des jours de ton serviteur? Quand feras-tu justice de mes persécuteurs?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Des orgueilleux creusent des fosses devant moi; ils n'agissent point d'après ta loi.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Tous tes commandements sont vrais: sans cause ils me persécutent; assiste-moi!
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Ils m'ont presque détruit, après m'avoir terrassé; mais je n'abandonne point tes commandements,
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Selon ta miséricorde rends-moi la vie, afin que j'observe les ordres de ta bouche! Lamed.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Éternellement, Seigneur, ta parole subsiste dans les Cieux,
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
d'âge en âge ta vérité demeure; tu as fondé la terre, et elle est stable;
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
suivant tes lois tout subsiste aujourd'hui, car toutes choses te sont assujetties.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Si ta loi n'eût fait mes délices, j'aurais péri dans ma misère.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Jamais je n'oublierai tes commandements, car c'est par eux que tu me fais vivre.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Je suis à toi: donne-moi ton secours! car je cherche tes commandements.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Les impies m'attendent pour me faire périr; je suis attentif à tes ordres.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
A toute chose parfaite j'ai vu une fin; ta loi est infinieMem.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Combien j'aime ta loi! elle est ma pensée de tous les jours.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Tes préceptes me rendent plus sage que mes ennemis. car ils sont toujours avec moi.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Je suis plus expert que tous mes maîtres, car tes ordonnances sont la pensée que j'ai;
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
je suis plus entendu que les vieillards, car j'observe tes commandements.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Je tiens mon pied loin de tout mauvais sentier, afin que j'observe ta parole.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Je ne m'écarte point de ta loi, car c'est toi qui m'instruis.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Que ta parole est douce à mon palais! elle l'est plus que le miel à ma bouche.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Dans tes commandements je puise l'intelligence, aussi je hais tous les sentiers du mensonge. Nun.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Ta parole est une lampe devant mes pieds, et une lumière sur mon sentier.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
J'ai fait le serment, et je le tiens, d'observer tes justes lois.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Je suis extrêmement affligé: Éternel, rends-moi la vie selon ta promesse!
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Agrée, Éternel, le libre hommage de ma bouche, et enseigne-moi tes lois!
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Ma vie est toujours en péril; mais je n'oublie point ta loi.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Des impies me tendent des pièges, mais je ne m'écarte point de tes ordres.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Je me suis pour toujours approprié tes préceptes car ils sont la joie de mon cœur.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
J'ai plié mon cœur à la pratique de tes lois, pour jamais, jusqu'à la fin. Samech.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Je hais les hommes partagés, et j'aime ta loi.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Tu es mon abri et mon bouclier; j'attends ta promesse.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Eloignez-vous de moi, méchants, afin que je garde les commandements de mon Dieu!
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Soutiens-moi selon ta promesse, afin que je vive, et ne me confonds point à cause de mon espoir!
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Sois mon appui, pour que je sois sauvé, et que j'aie toujours les yeux sur tes commandements!
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Tu méprises tous ceux qui s'écartent de tes lois; car leur fraude n'est qu'illusion.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Tu enlèves comme des scories tous les impies de la terre; c'est pourquoi j'aime tes ordonnances.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Tes terreurs font frissonner mon corps, et je redoute tes jugements. Aïn.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
J'ai pratiqué la loi, la justice: tu ne m'abandonneras pas à mes oppresseurs!
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Prends le parti de ton serviteur pour le sauver! que les superbes ne m'oppriment pas!
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mes yeux languissent après ton secours et ta juste promesse.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Traite ton serviteur selon ta miséricorde, et enseigne-moi tes ordonnances!
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Je suis ton serviteur: donne-moi l'intelligence, pour que j'aie la science de tes commandements.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Il est pour l'Éternel temps d'agir; ils ont enfreint ta loi.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Aussi j'aime tes commandements, plus que l'or, et que l'or pur;
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
aussi je trouve justes tous tes commandements; et je hais tous les sentiers du mensonge. Pé.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Tes commandements sont admirables; c'est pourquoi mon âme les garde.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
La révélation de tes paroles éclaire, donne de l'intelligence aux simples.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
J'ouvre la bouche, je soupire; car je suis avide de tes commandements.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Tourne tes regards sur moi, et prends pitié de moi, selon le droit de ceux qui aiment ton nom!
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Affermis mes pas dans ta parole, et ne laisse aucun mal prendre empire sur moi!
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Délivre-moi de l'oppression des hommes, afin que j'observe tes commandements!
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Fais luire ta face sur ton serviteur, et enseigne-moi tes ordonnances!
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Des torrents d'eau coulent de mes yeux, parce que l'on n'observe pas ta loi. Tsadé.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Tu es juste, Éternel, et tes jugements sont équitables;
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
tu prescris la justice dans tes ordonnances, et une grande vérité.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Mon indignation me consume, de ce que mes ennemis oublient tes paroles.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Ta parole est parfaitement pure, et ton serviteur l'aime.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Je suis chétif et méprisé; je n'oublie point tes préceptes.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Ta justice est un droit éternel, et ta loi, une vérité.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
La détresse et l'angoisse m'ont atteint; tes commandements sont mon délice.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
La justice de tes ordonnances est éternelle; donne-moi l'intelligence, afin que je vive! Quoph.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Je t'invoque de tout mon cœur, exauce-moi, Éternel afin que j'observe tes ordonnances!
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Je t'invoque: aide-moi, afin que je garde tes commandements!
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Je devance l'aurore et je crie; j'attends ta promesse.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Avant les veilles j'ouvre déjà les yeux, pour méditer ta parole.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Entends ma voix selon ta miséricorde! Éternel, selon ta justice donne-moi la vie!
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Ils s'approchent ceux qui poursuivent le mal, ils se tiennent loin de ta loi;
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
mais tu es proche, Éternel, et tous tes commandements sont vérité.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Dès longtemps je sais par tes décrets que pour l'éternité tu les as arrêtés. Resch.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Vois ma misère, et me délivre! car je n'oublie point ta loi.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Soutiens ma querelle, et me rachète! selon ta promesse donne-moi la vie!
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Le salut est loin des impies; car ils ne cherchent point tes ordonnances.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Tes compassions sont grandes, Éternel; donne-moi la vie selon tes décrets!
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Mes persécuteurs et mes oppresseurs sont nombreux; je n'ai point dévié de tes commandements.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Je vois les infidèles, et j'en ai de l'horreur; ils n'observent point ta parole.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Considère que j'aime tes commandements: Éternel, selon ta miséricorde donne-moi la vie!
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Le sommaire de ta parole, c'est vérité, et toutes tes justes lois sont éternelles. Schin.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Des princes me persécutent sans cause; mais mon cœur ne craint que tes paroles.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Je me réjouis de ta parole, comme celui qui trouve un grand butin.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Je hais, je déteste le mensonge; j'aime ta loi.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Sept fois le jour je te célèbre, à cause de tes justes lois.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Ils ont une grande paix ceux qui aiment la loi, pour eux il n'y a point de traverses.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Je m'attends à ton secours, Éternel, et je pratique tes commandements.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Mon âme observe tes ordonnances, et j'ai pour elles un grand amour.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
J'exécute tes ordres et tes commandements, car toutes mes voies sont présentes à tes yeux. Thav.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Que mes cris aient accès près de toi, Éternel! selon ta promesse donne-moi l'intelligence!
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Que ma prière arrive devant toi! selon ta promesse sauve-moi!
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Que mes lèvres épanchent la louange! car tu m'enseignes tous tes commandements!
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Que ma langue célèbre ta parole! car toutes tes lois sont justes.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Que ta main me soit en aide! car j'ai fait choix de tes commandements.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Je suis désireux de ton secours, Éternel, et ta loi fait mes délices.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Que mon âme vive, et qu'elle te loue! et de tes jugements donne-moi le secours!
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Je suis errant, comme une brebis perdue; cherche ton serviteur! car je n'oublie pas tes commandements.

< Masalimo 119 >