< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Alleluia. Confitemini Domino quoniam bonus: quoniam in sæculum misericordia eius.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Dicat nunc Israel quoniam bonus: quoniam in sæculum misericordia eius.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Dicat nunc domus Aaron: quoniam in sæculum misericordia eius.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Dicant nunc qui timent Dominum: quoniam in sæculum misericordia eius.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
De tribulatione invocavi Dominum: et exaudivit me in latitudine Dominus.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
Dominus mihi adiutor: non timebo quid faciat mihi homo.
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
Dominus mihi adiutor: et ego despiciam inimicos meos.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
Bonum est confidere in Domino, quam confidere in homine:
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
Bonum est sperare in Domino, quam sperare in principibus.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Omnes gentes circuierunt me: et in nomine Domini quia ultus sum in eos.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Circumdantes circumdederunt me: et in nomine Domini quia ultus sum in eos.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Circumdederunt me sicut apes, et exarserunt sicut ignis in spinis: et in nomine Domini quia ultus sum in eos.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Impulsus eversus sum ut caderem: et Dominus suscepit me.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
Fortitudo mea, et laus mea Dominus: et factus est mihi in salutem.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
Vox exultationis, et salutis in tabernaculis iustorum.
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
Dextera Domini fecit virtutem: dextera Domini exaltavit me, dextera Domini fecit virtutem.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
Non moriar, sed vivam: et narrabo opera Domini.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
Castigans castigavit me Dominus: et morti non tradidit me.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Aperite mihi portas iustitiæ, ingressus in eas confitebor Domino:
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
hæc porta Domini, iusti intrabunt in eam.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
Confitebor tibi quoniam exaudisti me: et factus es mihi in salutem.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
Lapidem, quem reprobaverunt ædificantes: hic factus est in caput anguli.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
A Domino factum est istud: et est mirabile in oculis nostris.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
Hæc est dies, quam fecit Dominus: exultemus, et lætemur in ea.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
O Domine salvum me fac, o Domine bene prosperare:
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
benedictus qui venit in nomine Domini. Benediximus vobis de domo Domini:
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
Deus Dominus, et illuxit nobis. Constituite diem solemnem in condensis, usque ad cornu altaris.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Deus meus es tu, et confitebor tibi: Deus meus es tu, et exaltabo te. Confitebor tibi quoniam exaudisti me: et factus es mihi in salutem.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Confitemini Domino quoniam bonus: quoniam in sæculum misericordia eius.

< Masalimo 118 >