< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Give thanks to the Lord for his goodness, his kindness endures forever.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let the house of Israel now say: his kindness endures forever.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let the house of Aaron now say: his kindness endures forever.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let those who fear the Lord now say: his kindness endures forever.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Out of straits I called on the Lord, the Lord answered and gave me room.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
The Lord is mine; I am fearless. What can mere people do to me?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
The Lord is mine, as my help: I shall feast my eyes on my foes.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
It is better to hide in the Lord than to trust in mortals.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
It is better to hide in the Lord than to put any trust in princes.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
Everywhere heathen swarmed round me; in the name of the Lord I cut them down.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
They swarmed, swarmed around me; in the name of the Lord I cut them down,
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
they swarmed around me like bees, they blazed like a fire of thorns: in the name of the Lord I cut them down.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Sore they pushed me, to make me fall; but the Lord gave me his help.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
The Lord is my strength and my song, and he is become my salvation.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
Hark! In the tents of the righteous glad cries of victory are ringing. The hand of the Lord has wrought bravely,
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
the hand of the Lord is exalted, the hand of the Lord has wrought bravely.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
I shall not die: nay, I shall live, to declare the works of the Lord.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
Though the Lord has chastened me sore, he has not given me over to death. (The Procession arrives at the Temple)
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
‘Open to me the gates of victory. I would enter therein and give thanks to the Lord.’ (The Welcome)
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
‘This is the gate of the Lord: the righteous may enter therein;’
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
I thank you because you have heard me, and are become my salvation.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
The stone which the builders despised is become the head-stone of the corner.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
This has been wrought by the Lord; it is marvellous in our eyes.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
This day is the Lord’s own creation: in it let us joy and be glad.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
O Lord, save us, we pray, O Lord, prosper, we pray.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Blessed the one who enters in the name of the Lord. From the house of the Lord we bless you.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
The Lord is God, he has given us light. Wreathe the dance with boughs, till they touch the horns of the altar.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
You are my God, I will thank you; O my God, I will exalt you.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
Give thanks to the Lord for his goodness: his kindness endures forever.

< Masalimo 118 >