< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Hallelujah. Praise the Lord, you his servants, praise the name of the Lord.
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
The name of the Lord be blessed from now and for evermore.
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
From sunrise to sunset is the name of the Lord to be praised.
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
High is the Lord above all nations, above the heavens is his glory.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Who is like the Lord our God, seated on high?
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
He bends down to look at the heavens and earth.
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
He raises the weak from the dust, he lifts the poor from the dunghill,
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
and sets them beside the princes, even the princes of his people.
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
He gives the childless woman a home, and makes her the happy mother of children. Hallelujah.

< Masalimo 113 >