< Masalimo 109 >

1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
Salmo de Davi, para o regente: Ó Deus a quem eu louvo, não fiques calado.
2 pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
Porque a boca do perverso, e a boca enganadora já se abriram contra mim; falaram de mim com língua falsa.
3 Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
E me cercaram com palavras de ódio; e lutaram contra mim sem motivo.
4 Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
Fizeram-se contra mim por causa de meu amor; porém eu [me mantenho] em oração.
5 Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
Retribuíram o bem com o mal, e o meu amor com ódio.
6 Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
Põe algum perverso contra ele, e que haja um acusador à sua direita.
7 Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
Quando for julgado, que saia condenado; e que a oração dele seja [considerada] como pecado.
8 Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
Sejam os dias dele poucos, e que outro tome sua atividade.
9 Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
Sejam seus filhos órfãos, e sua mulher seja viúva.
10 Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
E que seus filhos andem sem rumo, e mendiguem; e busquem [para si longe] de suas ruínas.
11 Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
Que o credor tome tudo o que ele tem, e estranhos saqueiem seu trabalho.
12 Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
Haja ninguém que tenha piedade dele, e haja ninguém que se compadeça de seus órfãos.
13 Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
Sejam seus descendentes cortados de vez; [e] que o nome deles seja apagado da geração seguinte.
14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
Que a perversidade de seus pais seja lembrada pelo SENHOR, e que o pecado de sua mãe não seja apagado.
15 Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
[Porém que tais coisas] estejam sempre perante o SENHOR, e corte-se a lembrança deles da terra.
16 Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
Porque ele não se lembrou de fazer o bem; ao invés disso, perseguiu ao homem humilde e necessitado, e ao de coração quebrado, para [o] matar.
17 Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
Já que ele amou a maldição, então que ela lhe sobrevenha; e já que ele não quis a bênção, que esta se afaste dele.
18 Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
E ele seja revestido de maldição, como se lhe fosse sua roupa, como água dentro do seu corpo, e como óleo em seus ossos.
19 Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
Que ela seja como uma roupa com que ele se cubra, e como cinto com que ele sempre põe ao seu redor.
20 Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
Isto seja o pagamento do SENHOR para os meus adversários, e para os que falam mal contra minha alma.
21 Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
Porém tu, Senhor DEUS, me trata [bem] por causa do teu nome; por ser boa a tua misericórdia, livra-me;
22 Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
Porque estou aflito e necessitado; e meu coração está ferido dentro de mim.
23 Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
Eu vou como a sombra, que declina; estou sendo sacudido como um gafanhoto.
24 Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
Meus joelhos estão fracos de [tanto] jejuar; minha carne está magra, sem gordura alguma.
25 Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
E eu por eles sou humilhado; quando me veem, sacodem suas cabeças.
26 Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
Socorre-me, SENHOR Deus meu; salva-me conforme a tua bondade;
27 Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
Para que saibam que esta é a tua mão; e que assim tu a fizeste.
28 Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
Maldigam eles, mas bendize tu; levantem-se eles, mas sejam envergonhados; e o teu servo se alegre.
29 Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
Que meus adversários se vistam de vergonha, e cubram-se com sua própria humilhação, como [se fosse] uma capa.
30 Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
Agradecerei grandemente ao SENHOR com minha boca, e no meio de muitos eu o louvarei;
31 Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.
Porque ele se põe à direita do necessitado, para [o] livrar daqueles que atacam a sua alma.

< Masalimo 109 >