< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Give thanks to the Lord, call on his name: make known his deeds among the nations.
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Sing to him, make music to him, tell of all his wondrous works.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Make your boast in his holy name, be glad at heart, you who seek the Lord.
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Seek after the Lord and his strength, seek his face evermore.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Remember the wonders he did, his portents, the judgments he uttered,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
you who are offspring of Abraham, his servant, the children of Jacob, his chosen ones.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
He is the Lord our God: in all the earth are his judgments.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
He remembers forever his covenant, his promise for a thousand generations
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
The covenant he made with Abraham, the oath he swore to Isaac,
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
and confirmed as a statute to Jacob, a pact everlasting to Israel
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
to give them the land of Canaan as the lot which they should inherit.
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
And when they were very few, few and but pilgrims therein,
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
wandering from nation to nation, journeying from people to people,
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
he allowed no one to oppress them, even punishing kings for their sakes.
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
He forbade them to touch his anointed, or do any hurt to his prophets.
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
When he called down famine on the land, and cut off the bread which sustained them,
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
he sent before them a man, Joseph, who was sold as a slave.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
His feet were galled with fetters, he was laid in chains of iron,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
till the time that his word came to pass, the word of the Lord that had tried him.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
The king sent and freed him, the ruler of nations released him.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
He made him lord of his household, and ruler of all his possessions,
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
to admonish his princes at will and instruct his elders in wisdom.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Thus Israel came into Egypt, Jacob sojourned in the land of Ham.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
His people he made very fruitful, and mightier than their foes.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
He inspired them to hate his people, and to deal with his servants craftily.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
He sent his servant Moses, and Aaron whom he had chosen,
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
portents he wrought in Egypt, and signs in the land of Ham.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Darkness he sent, and it fell: yet they gave no heed to his word.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
He turned their waters into blood, thus causing their fish to die.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Their land was alive with frogs, swarming even in the royal chambers.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
At his command came flies, and lice in all their borders.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
He gave them hail for rain and fire that flashed through the land,
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
smiting their vines and figs, breaking the trees of their border.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
At his command came locusts, young locusts beyond all counting,
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
which ate every herb in the land, ate up, too, the fruit of their ground.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
He struck down in their land all the firstborn, the firstlings of all their strength
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
Then forth he led Israel with silver and gold, and among his tribes no one was weary.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Egypt was glad when they left, for terror had fallen upon them.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
He spread out a cloud to screen them, and fire to give light in the night.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
He sent quails at their entreaty, and heavenly bread in abundance.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
He opened the rock; waters gushed: in the desert they ran like a river.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
For he remembered his holy promise to Abraham his servant.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
So he led out his people with joy, his elect with a ringing cry.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
And he gave them the lands of the nations, the fruit of their toil for possession,
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
that so they might keep his statutes, and be of his laws observant. Hallelujah.

< Masalimo 105 >