< Masalimo 104 >

1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
Aw ka hqingnaak, Bawipa kyihcah lah. Aw Bawipa ka Khawsa, nang taw bau soeih hyk ti; boeimang ypawmnaak ing thoeihcam qu hyk ti.
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
Vangnaak ce hi amyihna bai nawh; khankhqi ce hi im amyihna phyl hy,
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
a awmnaak ak khan ipkaikhqi ce tuikhqik khan awh zilh ang hlakhqi awh ce ngawi hy.
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
Zilh ce a ceityihkhqi na sai nawh; maikqawng ing mai ce a tyihzawih na sai hy.
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
Khawmdek ve ang hangnaak hun awh hawih nawh, am thoeih qoe hy.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
Tuihdung ingkaw hi amyihna zawl malh nawh; tlangkhqi ak khan awh tui pha sak hyk ti.
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
Cehlai nang ing na zyih a dawngawh tuikhqi cen nawh, nang a khawhum awi awh ang tawnna cen hy;
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
tlangkhqik khanna lawng unawh tuikawkhqi awh awm nung lawng uhy, a mingmih aham hun na qoek na bah peeknaak hun awh lawng uhy.
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Cekkhqi amang lawngnaak thai aham qamqi taak pe hyk ti; ityk awh awm khawmdek ve am leu voel tikaw.
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
Lawngsip awm sak nawh lawnghawi dung awh lawng sak hy; tlangkhqi anglakawh ce lawng hy.
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
Qam awhkaw chukphakhqi boeih ce awk sak nawh; kqawng meqangkhqi ami tui ngaih sit hy.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
Khan nakaw phakhqi ing tuikeng awh bu sawn unawh; thingpangkhqi awh laa sa uhy.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
A awmnaak aham im awhkawng tlangkhqi ce tui ing syp nawh; a bibinaak ak thaih ing khawmdek ve phoen phyi sak hy.
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
Khqin aham qam cawn sak nawh, thlanghqing aham tawihah anhah cawt sak hy – khawmdek awhkawng buh a an taak law pehy:
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
thlang ak kawlung ak zeel sak misur tui, haai a plangnaak aham situi, ak kawlung tha ak awm sak phaihpi ce pehy.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
Bawipa a thingkhqi, Lebanon awh amah ing ang lingkhqi ce khaw ing ak qui na syp hy.
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
Cawh phakhqi ing bu sawn unawh, sidar a thing awh phungawkhqi ing im ta uhy.
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
Tlang sangkhqi cetaw sangza sithai awmnaak hun na awm nawh; minpoengkhqi cetaw phihkhqi a awmnaak hun na awm hy.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
Hla ing khawcan sim nawh, khawmik ing a nung tlaak tym sim hy.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Nang ing thannaak haw law tiksaw, khawmthan na coeng hy, cawh khqinkhqi lym ang hang uhy.
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
Sendeihkhqi ing khqin a ai kawi tu aham ami ngaih awh kawk unawh, Khawsa venawh kawng ai sui uhy.
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
Khawmik ang thoeng law awhtaw qeng sap uhy; a awmnaak lukkawk khuina voei unawh zaih uhy.
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
Cawh thlang ing bibi aham cet nawh, khawmy dy bi sai hy.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
Aw Bawipa, na bibi ve kqeng soeih mah hy! Cyihnaak ing vemyihkhqi boeih ve sai hyk ti; khawmdek ve na sai ik-oeih ing bengen hy.
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
Ak kau soeih tuicunli awm awm nawh, noet noeng kaana a sai lumngakhqi ak zawi ak bau awm hy.
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
Cawh lawk baukhqi hu hai na cet unawh, cawh nang ing tuinga ang lymnaak khoek hun ce sai pe hyk ti.
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
A tym can awh nang ing buh na peek hly ce lamtoen doena nang ce ni toek uhy.
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
Cekkhqi ce buh na peek awh, a mingmih ing cung hloep uhy, nang ing na kut nak thlek awh cekkhqi ing ik-oeik leek ing be uhy.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
Cehlai haai na thuh awh, mawn uhy; cekkhqi ang hqi ce na lawh peek valh awh, thi unawh dekvai na hlat uhy.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
Nang Myihla ce na tyih awh, a mingmih ce sai na awm unawh, nang ing khawmdek ce tlaih pan hyk ti.
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
Bawipa a boeimangnaak taw kumqui dy awm poe seh; a bibinaak awh Bawipa taw zeel seh –
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
khawmdek toek nawh, tyn sak hy, tlangkhqi bi nawh khu sak hy.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
Ka hqing khui pyt Bawipa venawh laa sa kawng nyng; ka hqing khui ka Khawsa kyihcahnaak laa sa vang nyng.
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
Bawipa awh ka zeel lawt amyihna, kak kawpoeknaak ve a venawh zeelnaak na awm seh.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
Cehlai thlak thawlhkhqi taw khawmdek awhkawng cing baat u seitaw thlakchekhqi awm koeh awm voel u seh. Aw ka hqingnaak, Bawipa ce kyihcah lah.

< Masalimo 104 >