< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
Ein Gebet des Elenden, so er betrübt ist und seine Klage vor dem HERRN ausschüttet. HERR, höre mein Gebet und laß mein Schreien zu dir kommen!
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
Verbirg dein Antlitz nicht vor mir in der Not; neige deine Ohren zu mir; wenn ich dich anrufe, so erhöre mich bald!
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
Denn meine Tage sind vergangen wie ein Rauch, und meine Gebeine sind verbrannt wie ein Brand.
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
Mein Herz ist geschlagen und verdorret wie Gras, daß ich auch vergesse, mein Brot zu essen.
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Mein Gebein klebt an meinem Fleisch vor Heulen und Seufzen.
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
Ich bin gleich wie eine Rohrdommel in der Wüste; ich bin gleich wie ein Käuzlein in den verstörten Stätten.
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
Ich wache und bin wie ein einsamer Vogel auf dem Dache.
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Täglich schmähen mich meine Feinde; und die mich spotten, schwören bei mir.
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
Denn ich esse Asche wie Brot und mische meinen Trank mit Weinen
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
vor deinem Dräuen und Zorn, daß du mich aufgehoben und zu Boden gestoßen hast.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
Meine Tage sind dahin wie ein Schatten; und ich verdorre wie Gras.
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
Du aber, HERR, bleibest ewiglich und dein Gedächtnis für und für.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
Du wollest dich aufmachen und über Zion erbarmen; denn es ist Zeit, daß du ihr gnädig seiest, und die Stunde ist kommen.
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
Denn deine Knechte wollten gerne, daß sie gebauet würde, und sähen gerne, daß ihre Steine und Kalk zugerichtet würden;
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
daß die Heiden den Namen des HERRN fürchten und alle Könige auf Erden deine Ehre;
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
daß der HERR Zion bauet und erscheinet in seiner Ehre.
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
Er wendet sich zum Gebet der Verlassenen und verschmähet ihr Gebet nicht.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
Das werde geschrieben auf die Nachkommen; und das Volk, das geschaffen soll werden, wird den HERRN loben.
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
Denn er schauet von seiner heiligen Höhe, und der HERR siehet vom Himmel auf Erden,
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
daß er das Seufzen des Gefangenen höre und losmache die Kinder des Todes,
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
auf daß sie zu Zion predigen den Namen des HERRN und sein Lob zu Jerusalem,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
wenn die Völker zusammenkommen und die Königreiche, dem HERRN zu dienen.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
Er demütiget auf dem Wege meine Kraft; er verkürzet meine Tage.
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
Ich sage: Mein Gott, nimm mich nicht weg in der Hälfte meiner Tage! Deine Jahre währen für und für.
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
Du hast vorhin die Erde gegründet, und die Himmel sind deiner Hände Werk.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
Sie werden vergehen, aber du bleibest. Sie werden alle veralten wie ein Gewand; sie werden verwandelt wie ein Kleid, wenn du sie verwandeln wirst.
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
Du aber bleibest, wie du bist, und deine Jahre nehmen kein Ende.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

< Masalimo 102 >