< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
Aw Bawipa, kak cykcahnaak awi ve ngai law lah; bawm aham kang kqang awi ve na ven pha seh.
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
Ka khuikha awh ve na haai koeh thuh. Kai benna nang haa keng law nawhtaw; ka nik khy awh ang tawnna nim hlat lah.
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
Ka hqing khui khawnghikhqi ve maikhu amyihna ding bang nawh; ka quhkhqi ve maialh amyihna alh hy.
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
Kak kawlung ve koh aai nawh qam amyihna reu hy; buh ai aham awm hilh qu hawh nyng.
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Kang ko awh ka quh ingkaw ka vyn hqawng ni ak awm hqoeng hawh.
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
Qamkoh awhkaw bukbu amyihna ngawi hqoeng nyng saw, ak plawci anglakawhkaw bukbu amyihna awm hqoeng nyng.
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
Ihmyh lonai na awm nyng saw; iptih khanna amah doeng ak ngawi hqoeng pha amyihna awm nyng.
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
Khawnghi zung ka qaalkhqi ing nik kqawnset unawh, kai anik huhqytkhqi ing kang ming ve kqawn setnaak na hawna uhy.
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
Maivytkhqi ce buh na ai nyng saw ka awk hly kawi awm mikphli tuikhqi ing kqit uhy,
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
nak kaw a so aih awh, ni lo hqoet nawh nik khawng hyk ti.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
Ka hqingnaak khawnghikhqi ve khawmy benna kaw khawngkawn amyihna awm nawh; qam amyihna reu hy.
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
Cehlai, Bawipa, nang taw kumqui dy boei ngawihdoelh awh ngawi hyk ti; nang ming awm cadil naa dyna cak hy.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
Nang tho kawm tiksaw Zion ce qeen kawp ti, anih a venawh zeelnaak tym qoe hawh ni; a tym a taak ce pha law hawh hy.
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
Na ceityihkhqi ing anih a lung ce lungna unawh; a dekvai ing cekkhqi ce am thin tlawh sak hy.
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
Phynlumkhqi ing Bawipang ming kqih kawm usaw, khawmdek awhkaw sangpahrangkhqi boeih ing na boeimangnaak ce kqihchah kawm uh.
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
Ikawtih Bawipa ing Zion ce sa tlaih kawmsaw a boeimangnaak ing dang tlaih kaw.
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
Khawdeng ak voethlauhkhqi ak cykcahnaak ce hlat pe kaw; cekkhqi a qeen thoehnaak ce am huhsit pek khqi tikaw.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
Ve ve ak law hly kawi cadil naakhqi ham qee na awm seh; saina ak awm hlankhqi ing Bawipa ce kyihcah na seh.
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
Bawipa ing a hun ciim sang soeih awhkawng nuk toek hy, khan nakawng khawmdek ve nuk toek hy,
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
thawng ak tlakhqi a ko kqangnaak awi ce ngai peek aham ingkaw thih aham ami palh sak thlangkhqi ce loet sak aham.”
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
Bawipang ming ce Zion awh kqawn na awm kawmsaw am kyihnaak ce Jerusalem awh awm kaw,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
thlangkhqi ingkaw qamkhqi ing Bawipa bawk aham cawn kawm uh.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
Khaw ka sak pyngthym mai awh kak tha ni boek pe nawh; ka hqinglung ni tawi pe sak hy.
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
Cedawngawh kai ing, Aw ka Khawsa, ka hqing huili awh koeh ni lo valh; nang a kumkhqi taw cadil naa dyna ak awm ni.
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
Ak cykca awh nang ing khawmdek pengnelhnaak sai tiksaw, khankhqi ce na kut ing sai na awm hy.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
Ceekhqi taw qeng hlai voei uh, nang taw awm poe kawp ti; cekkhqi taw hi amyihna se kawm uh. Bainaak amyihna thaw kawm tiksaw lawha boeih kaw.
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
Cehlai nang taw amah toeng na awm poe kawp ti, nang a kumkhqi ingtaw a dytnaak awm am ti kaw.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
A tyihzawihkhqi a cakhqi ce na haiawh awm kawm usaw; a cadilkhqi awm na haiawh cak poe hawh kawm uh.”

< Masalimo 102 >