< Miyambo 7 >

1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
Fili mi, custodi sermones meos, et præcepta mea reconde tibi. Fili,
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
serva mandata mea, et vives; et legem meam quasi pupillam oculi tui:
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
liga eam in digitis tuis, scribe illam in tabulis cordis tui.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Dic sapientiæ: Soror mea es, et prudentiam voca amicam tuam:
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
ut custodiant te a muliere extranea, et ab aliena quæ verba sua dulcia facit.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
De fenestra enim domus meæ per cancellos prospexi,
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
et video parvulos; considero vecordem juvenem,
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
qui transit per plateam juxta angulum et prope viam domus illius graditur:
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
in obscuro, advesperascente die, in noctis tenebris et caligine.
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
Et ecce occurrit illi mulier ornatu meretricio, præparata ad capiendas animas: garrula et vaga,
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
quietis impatiens, nec valens in domo consistere pedibus suis;
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
nunc foris, nunc in plateis, nunc juxta angulos insidians.
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
Apprehensumque deosculatur juvenem, et procaci vultu blanditur, dicens:
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
Victimas pro salute vovi; hodie reddidi vota mea:
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
idcirco egressa sum in occursum tuum, desiderans te videre, et reperi.
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
Intexui funibus lectulum meum; stravi tapetibus pictis ex Ægypto:
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
aspersi cubile meum myrrha, et aloë, et cinnamomo.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Veni, inebriemur uberibus, et fruamur cupitis amplexibus donec illucescat dies.
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
Non est enim vir in domo sua: abiit via longissima:
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
sacculum pecuniæ secum tulit; in die plenæ lunæ reversurus est in domum suam.
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
Irretivit eum multis sermonibus, et blanditiis labiorum protraxit illum.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
Statim eam sequitur quasi bos ductus ad victimam, et quasi agnus lasciviens, et ignorans quod ad vincula stultus trahatur:
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
donec transfigat sagitta jecur ejus, velut si avis festinet ad laqueum, et nescit quod de periculo animæ illius agitur.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Nunc ergo, fili mi, audi me, et attende verbis oris mei.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
Ne abstrahatur in viis illius mens tua, neque decipiaris semitis ejus;
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
multos enim vulneratos dejecit, et fortissimi quique interfecti sunt ab ea.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)
Viæ inferi domus ejus, penetrantes in interiora mortis. (Sheol h7585)

< Miyambo 7 >