< Miyambo 31 >

1 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
The wordis of Lamuel, the king; the visioun bi which his modir tauyte hym.
2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
What my derlyng? what the derlyng of my wombe? what the derlyng of my desiris?
3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
Yyue thou not thi catel to wymmen, and thi richessis to do awei kyngis.
4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
A! Lamuel, nyle thou yiue wyn to kingis; for no pryuete is, where drunkenesse regneth.
5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
Lest perauenture thei drynke, and foryete domes, and chaunge the cause of the sones of a pore man.
6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
Yyue ye sidur to hem that morenen, and wyn to hem that ben of bitter soule.
7 amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
Drinke thei, and foryete thei her nedinesse; and thenke thei no more on her sorewe.
8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
Opene thi mouth for a doumb man,
9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
and opene thi mouth for the causes of alle sones that passen forth. Deme thou that that is iust, and deme thou a nedi man and a pore man.
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
Who schal fynde a stronge womman? the prijs of her is fer, and fro the laste endis.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
The herte of hir hosebond tristith in hir; and sche schal not haue nede to spuylis.
12 Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
Sche schal yelde to hym good, and not yuel, in alle the daies of hir lijf.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
Sche souyte wolle and flex; and wrouyte bi the counsel of hir hondis.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
Sche is maad as the schip of a marchaunt, that berith his breed fro fer.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
And sche roos bi nyyt, and yaf prey to hir meyneals, and metis to hir handmaidis.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
Sche bihelde a feeld, and bouyte it; of the fruyt of hir hondis sche plauntide a vyner.
17 Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
Sche girde hir leendis with strengthe, and made strong hir arm.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
Sche taastide, and siy, that hir marchaundie was good; hir lanterne schal not be quenchid in the niyt.
19 Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
Sche putte hir hondis to stronge thingis, and hir fyngris token the spyndil.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
Sche openyde hir hond to a nedi man, and stretchide forth hir hondis to a pore man.
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
Sche schal not drede for hir hous of the cooldis of snow; for alle hir meyneals ben clothid with double clothis.
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
Sche made to hir a ray cloth; bijs and purpur is the cloth of hir.
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
Hir hosebonde is noble in the yatis, whanne he sittith with the senatours of erthe.
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
Sche made lynnun cloth, and selde; and yaf a girdil to a Chananei.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
Strengthe and fairnesse is the clothing of hir; and sche schal leiye in the laste dai.
26 Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
Sche openyde hir mouth to wisdom; and the lawe of merci is in hir tunge.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
Sche bihelde the pathis of hir hous; and sche eet not breed idili.
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
Hir sones risiden, and prechiden hir moost blessid; hir hosebonde roos, and preiside hir.
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
Many douytris gaderiden richessis; thou passidist alle.
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
Fairnesse is disseiuable grace, and veyn; thilke womman, that dredith the Lord, schal be preisid.
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.
Yyue ye to hir of the fruyt of hir hondis; and hir werkis preise hir in the yatis.

< Miyambo 31 >