< Miyambo 30 >

1 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
The words of Agur the son of Jakeh, the revelation: the man says to Ithiel, to Ithiel and Ucal:
2 “Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
“Surely I am the most ignorant man, and don’t have a man’s understanding.
3 Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
I have not learned wisdom, neither do I have the knowledge of the Holy One.
4 Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
Who has ascended up into heaven, and descended? Who has gathered the wind in his fists? Who has bound the waters in his garment? Who has established all the ends of the earth? What is his name, and what is his son’s name, if you know?
5 “Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
“Every word of God is flawless. He is a shield to those who take refuge in him.
6 Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
Don’t you add to his words, lest he reprove you, and you be found a liar.
7 “Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
“Two things I have asked of you. Don’t deny me before I die.
8 Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
Remove far from me falsehood and lies. Give me neither poverty nor riches. Feed me with the food that is needful for me,
9 kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
lest I be full, deny you, and say, ‘Who is the LORD?’ or lest I be poor, and steal, and so dishonor the name of my God.
10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
“Don’t slander a servant to his master, lest he curse you, and you be held guilty.
11 “Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
There is a generation that curses their father, and doesn’t bless their mother.
12 Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
There is a generation that is pure in their own eyes, yet are not washed from their filthiness.
13 Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
There is a generation, oh how lofty are their eyes! Their eyelids are lifted up.
14 Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
There is a generation whose teeth are like swords, and their jaws like knives, to devour the poor from the earth, and the needy from among men.
15 “Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
“The leech has two daughters: ‘Give, give.’ “There are three things that are never satisfied; four that don’t say, ‘Enough!’:
16 Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
Sheol, the barren womb, the earth that is not satisfied with water, and the fire that doesn’t say, ‘Enough!’ (Sheol h7585)
17 Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
“The eye that mocks at his father, and scorns obedience to his mother, the ravens of the valley shall pick it out, the young eagles shall eat it.
18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
“There are three things which are too amazing for me, four which I don’t understand:
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
The way of an eagle in the air, the way of a serpent on a rock, the way of a ship in the middle of the sea, and the way of a man with a maiden.
20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
“So is the way of an adulterous woman: She eats and wipes her mouth, and says, ‘I have done nothing wrong.’
21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
“For three things the earth trembles, and under four, it can’t bear up:
22 Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
For a servant when he is king, a fool when he is filled with food,
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
for an unloved woman when she is married, and a servant who is heir to her mistress.
24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
“There are four things which are little on the earth, but they are exceedingly wise:
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
The ants are not a strong people, yet they provide their food in the summer.
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
The hyraxes are but a feeble folk, yet make they their houses in the rocks.
27 dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
The locusts have no king, yet they advance in ranks.
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
You can catch a lizard with your hands, yet it is in kings’ palaces.
29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
“There are three things which are stately in their march, four which are stately in going:
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
The lion, which is mightiest among animals, and doesn’t turn away for any;
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
the greyhound; the male goat; and the king against whom there is no rising up.
32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
“If you have done foolishly in lifting up yourself, or if you have thought evil, put your hand over your mouth.
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”
For as the churning of milk produces butter, and the wringing of the nose produces blood, so the forcing of wrath produces strife.”

< Miyambo 30 >