< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
My son, do not forget my teaching; but let your heart keep my commandments:
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
for length of days, and years of life, and peace, will they add to you.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Do not let kindness and truth forsake you. Bind them around your neck. Write them on the tablet of your heart.
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
So you will find favor, and good understanding in the sight of God and man.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Trust in YHWH with all your heart, and do not lean on your own understanding.
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
In all your ways remember him, and he will make your paths straight.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Do not be wise in your own eyes. Fear YHWH, and depart from evil.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
It will be health to your body, and nourishment to your bones.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Honor YHWH with your substance, with the first fruits of all your increase:
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
so your storehouses will be filled with plenty, and your vats will overflow with new wine.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
My son, do not despise the discipline of YHWH, nor resent his correction.
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
For whom YHWH loves he disciplines, and punishes every son he accepts.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Blessed is the man who finds wisdom, the man who gets understanding.
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
For her good profit is better than getting silver, and her return is better than fine gold.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
She is more precious than rubies. None of the things you can desire are to be compared to her.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Length of days is in her right hand. In her left hand are riches and honor.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
Her ways are ways of pleasantness. All her paths are peace.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
She is a tree of life to those who lay hold of her, and those who hold on to her are blessed
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
By wisdom YHWH founded the earth. By understanding, he established the heavens.
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
By his knowledge, the depths were broken up, and the skies drop down the dew.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
My son, let them not depart from your eyes. Keep sound wisdom and discretion:
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
so they will be life to your soul, and grace for your neck.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Then you shall walk in your way securely, and your foot won't stumble.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
When you lie down, you will not be afraid; you will lie down, and your sleep will be sweet.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Do not be afraid of sudden fear, or of the storm of the wicked when it comes:
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
for YHWH will be your confidence, and will keep your foot from being taken.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Do not withhold good from those to whom it is due, when it is in the power of your hand to do it.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Do not say to your neighbor, "Go, and come again; tomorrow I will give it to you," when you have it by you.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Do not devise evil against your neighbor, seeing he dwells securely by you.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Do not strive with a man without cause, if he has done you no harm.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Do not envy the man of violence. Choose none of his ways.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
For the perverse is an abomination to YHWH, but his friendship is with the upright.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
YHWH's curse is in the house of the wicked, but he blesses the habitation of the righteous.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Surely he is scornful to scoffers, but he gives grace to the humble.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
The wise will inherit glory, but shame will be the promotion of fools.

< Miyambo 3 >