< Miyambo 29 >

1 Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
A man that hardeneth his necke when he is rebuked, shall suddenly be destroyed and can not be cured.
2 Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
When the righteous are in authoritie, the people reioyce: but when the wicked beareth rule, the people sigh.
3 Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
A man that loueth wisdome, reioyceth his father: but he that feedeth harlots, wasteth his substance.
4 Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
A King by iudgement mainteineth ye countrey: but a man receiuing giftes, destroyeth it.
5 Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
A man that flattereth his neighbour, spreadeth a net for his steps.
6 Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
In the transgression of an euill man is his snare: but the righteous doeth sing and reioyce.
7 Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
The righteous knoweth the cause of the poore: but the wicked regardeth not knowledge.
8 Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
Scornefull men bring a citie into a snare: but wise men turne away wrath.
9 Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
If a wise man contend with a foolish man, whether he be angry or laugh, there is no rest.
10 Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
Bloodie men hate him that is vpright: but the iust haue care of his soule.
11 Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
A foole powreth out all his minde: but a wise man keepeth it in till afterward.
12 Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
Of a prince that hearkeneth to lyes, all his seruants are wicked.
13 Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
The poore and the vsurer meete together, and the Lord lighteneth both their eyes.
14 Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
A King that iudgeth the poore in trueth, his throne shalbe established for euer.
15 Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
The rodde and correction giue wisdome: but a childe set a libertie, maketh his mother ashamed.
16 Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
When the wicked are increased, transgression increaseth: but ye righteous shall see their fall.
17 Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
Correct thy sonne and he will giue thee rest, and will giue pleasures to thy soule.
18 Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
Where there is no vision, the people decay: but he that keepeth the Lawe, is blessed.
19 Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
A seruant will not be chastised with words: though he vnderstand, yet he will not answere.
20 Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
Seest thou a man hastie in his matters? there is more hope of a foole, then of him.
21 Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
He that delicately bringeth vp his seruant from youth, at length he will be euen as his sone.
22 Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
An angrie man stirreth vp strife, and a furious man aboundeth in transgression.
23 Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
The pride of a man shall bring him lowe: but the humble in spirit shall enioy glory.
24 Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
He that is partner with a thiefe, hateth his owne soule: he heareth cursing, and declareth it not.
25 Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
The feare of man bringeth a snare: but he that trusteth in the Lord, shalbe exalted.
26 Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
Many doe seeke the face of the ruler: but euery mans iudgement commeth from the Lord.
27 Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.
A wicked man is abomination to the iust, and he that is vpright in his way, is abomination to the wicked.

< Miyambo 29 >