< Miyambo 25 >

1 Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
These, too, are parables of Solomon, which the men of Hezekiah, king of Judah, transferred.
2 Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
It is to the glory of God to conceal a word, and it is to the glory of kings to investigate speech.
3 Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
Heaven above, and earth below, and the heart of kings are each unsearchable.
4 Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
Take away the tarnish from silver, and a most pure vessel will go forth.
5 Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
Take away impiety from the face of the king, and his throne shall be made firm by justice.
6 Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
Do not appear glorious before the king, and do not stand in the place of the great.
7 paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
For it is better that it should be said to you, “Ascend to here,” than that you should be humbled before the prince.
8 usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
The things that your eyes have seen, do not offer hastily in a quarrel, lest afterward you may not be able to make amends, when you have dishonored your friend.
9 Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
Argue your case with your friend, and do not reveal the secret to an outsider,
10 kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
lest perhaps he may insult you, when he has heard it, and he might not cease to reproach you. Grace and friendship free a man; preserve these for yourself, lest you fall under reproach.
11 Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
Whoever speaks a word at an opportune time is like apples of gold on beds of silver.
12 Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
Whoever reproves the wise and obedient ear is like an earring of gold with a shining pearl.
13 Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
Just like the cold of snow in a time of harvest, so also is a faithful messenger to him who sent him: he causes his soul to rest.
14 Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
A man who boasts and does not fulfill his promises is like clouds and wind, when rain does not follow.
15 Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
By patience, a leader shall be appeased, and a soft tongue shall break hardness.
16 Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
You have discovered honey; eat what is sufficient for you, lest perhaps, being filled up, you may vomit it.
17 Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
Withdraw your feet from the house of your neighbor, lest, when he has had his fill, he may hate you.
18 Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
A man who speaks false testimony against his neighbor is like a dart and a sword and a sharp arrow.
19 Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
Whoever sets his hopes on the unfaithful in a day of anguish is like a rotten tooth and weary foot,
20 Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
and like one who loosens his garment in cold weather. Whoever sings verses to a wicked heart is like vinegar on baking soda. Just like a moth to a garment, and a worm to wood, so too does the sadness of a man do harm to the heart.
21 Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
If your enemy is hungry, feed him. If he is thirsty, give him water to drink.
22 Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
For you will gather hot coals upon his head, and the Lord will repay you.
23 Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
The north wind brings forth the rain, and a sorrowful face brings forth a detracting tongue.
24 Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
It is better to sit in a corner of the attic, than with an argumentative woman and in a shared house.
25 Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
Like cold water to a thirsty soul, so too are good reports from a far away land.
26 Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
The just falling down before the impious is like a fountain stirred up by feet and like a corrupted spring.
27 Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
Just as whoever eats too much honey, it is not good for him, so also whoever is an investigator of what is majestic will be overwhelmed by glory.
28 Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.
Just like a city lying in the open and without surrounding walls, so also is a man who is unable to restrain his own spirit in speaking.

< Miyambo 25 >